< Isaiah 32 >
1 Behold, a King shall reigne in iustice, and the princes shall rule in iudgement.
Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2 And that man shall bee as an hiding place from the winde, and as a refuge for the tempest: as riuers of water in a drie place, and as the shadowe of a great rocke in a weary land.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3 The eyes of the seeing shall not be shut, and the eares of them that heare, shall hearken.
Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4 And the heart of the foolish shall vnderstand knowledge, and the tongue of the stutters shalbe ready to speake distinctly.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5 A nigard shall no more be called liberall, nor the churle riche.
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6 But the nigarde will speake of nigardnesse, and his heart will worke iniquitie, and do wickedly, and speake falsely against the Lord, to make emptie the hungrie soule, and to cause the drinke of the thirstie to faile.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7 For the weapons of the churle are wicked: hee deuiseth wicked counsels, to vndoe the poore with lying words: and to speake against the poore in iudgement.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8 But the liberall man will deuise of liberall things, and he will continue his liberalitie.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
9 Rise vp, ye women that are at ease: heare my voyce, ye carelesse daughters: hearken to my wordes.
Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Yee women, that are carelesse, shall be in feare aboue a yeere in dayes: for the vintage shall faile, and the gatherings shall come no more.
Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Yee women, that are at ease, be astonied: feare, O yee carelesse women: put off the clothes: make bare, and girde sackcloth vpon the loynes.
Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 Men shall lament for the teates, euen for the pleasant fieldes, and for the fruitefull vine.
Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
13 Vpon the lande of my people shall growe thornes and briers: yea, vpon all the houses of ioye in the citie of reioysing,
Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Because the palace shalbe forsaken, and the noise of the citie shalbe left: the towre and fortresse shalbe dennes for euer, and the delite of wilde asses, and a pasture for flockes,
Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 Vntill the Spirit be powred vpon vs from aboue, and the wildernes become a fruitfull fielde, and the plenteous fielde be counted as a forest.
Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 And iudgement shall dwel in the desert, and iustice shall remaine in the fruitfull fielde.
Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 And the worke of iustice shall bee peace, euen the worke of iustice and quietnesse, and assurance for euer.
Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 And my people shall dwell in the tabernacle of peace, and in sure dwellings, and in safe resting places.
Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 When it haileth, it shall fall on the forest, and the citie shall be set in the lowe place.
Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 Blessed are ye that sowe vpon all waters, and driue thither the feete of the oxe and the asse.
inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.