< Isaiah 31 >

1 Woe vnto them that goe downe into Egypt for helpe, and stay vpon horses, and trust in charets, because they are many, and in horsemen, because they be very strong: but they looke not vnto the holy one of Israel, nor seeke vnto the Lord.
Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
2 But he yet is wisest: therefore he wil bring euill, and not turne backe his worde, but he will arise against the house of the wicked, and against the helpe of them that worke vanitie.
Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
3 Now the Egyptians are men, and not God, and their horses flesh and not spirite: and when the Lord shall stretch out his hand, the helper shall fall, and hee that is holpen shall fall, and they shall altogether faile.
Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
4 For thus hath the Lord spoken vnto me, As the lyon or lyons whelpe roareth vpon his praye, against whom if a multitude of shepheards be called, hee will not be afraide at their voyce, neither will humble him selfe at their noise: so shall the Lord of hostes come downe to fight for mount Zion, and for the hill thereof.
Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
5 As birds that flie, so shall the Lord of hostes defend Ierusalem by defending and deliuering, by passing through and preseruing it.
Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
6 O ye children of Israel, turne againe, in as much as ye are sunken deepe in rebellion.
Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
7 For in that day euery man shall cast out his idoles of siluer, and his idoles of golde, which your handes haue made you, euen a sinne.
Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
8 Then shall Asshur fall by the sworde, not of man, neither shall the sworde of man deuoure him, and hee shall flee from the sworde, and his yong men shall faint.
“Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
9 And he shall go for feare to his towre, and his princes shall be afraide of the standart, sayeth the Lord, whose fire is in Zion, and his fornace in Ierusalem.
Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.

< Isaiah 31 >