< Isaiah 19 >
1 The burden of Egypt. Beholde, the Lord rideth vpon a swift cloude, and shall come into Egypt, and the idoles of Egypt shall be moued at his presence, and the heart of Egypt shall melt in the middes of her.
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 And I will set the Egyptians against the Egyptians: so euery one shall fight against his brother, and euery one against his neighbour, citie against citie, and kingdome against kingdome.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 And the spirite of Egypt shall faile in the middes of her, and I will destroy their counsell, and they shall seeke at the idoles, and at the sorcerers, and at them that haue spirits of diuination, and at the southsayers.
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 And I will deliuer the Egyptians into the hand of the cruell Lordes, and a mightie King shall rule ouer them, sayth the Lord God of hostes.
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 Then the waters of the sea shall faile, and the riuers shall be dryed vp, and wasted.
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 And the riuers shall goe farre away: the riuers of defence shalbe emptied and dryed vp: the reedes and flagges shall be cut downe.
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 The grasse in the riuer, and at the head of the riuers, and all that groweth by the riuer, shall wither, and be driuen away, and be no more.
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 The fishers also shall mourne, and all they that cast angle into the riuer, shall lament, and they that spread their nette vpon the waters, shall be weakened.
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 Moreouer, they that worke in flaxe of diuers sortes, shall be confounded, and they that weaue nettes.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 For their nettes shalbe broken, and all they, that make pondes, shalbe heauie in heart.
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 Surely the princes of Zoan are fooles: the counsell of the wise counselers of Pharaoh is become foolish: how say ye vnto Pharaoh, I am the sonne of the wise? I am the sonne of the ancient Kings?
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Where are nowe thy wise men, that they may tell thee, or may knowe what the Lord of hostes hath determined against Egypt?
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 The princes of Zoan are become fooles: the princes of Noph are deceiued, they haue deceiued Egypt, euen the corners of the tribes thereof.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 The Lord hath mingled among them the spirite of errours: and they haue caused Egypt to erre in euery worke thereof, as a drunken man erreth in his vomite.
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 Neither shall there be any worke in Egypt, which the head may doe, nor the tayle, ye branch nor the rush.
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 In that day shall Egypt be like vnto women: for it shall be afraide and feare because of the moouing of the hand of the Lord of hostes, which he shaketh ouer it.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 And the land of Iudah shall be a feare vnto Egypt: euery one that maketh mention of it, shalbe afraid thereat, because of ye counsell of the Lord of hostes, which he hath determined vpon it.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 In that day shall fiue cities in the lande of Egypt speake the language of Canaan, and shall sweare by the Lord of hostes. one shall be called the citie of destruction.
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 In that day shall the altar of the Lord be in the middes of the land of Egypt, and a pillar by the border thereof vnto the Lord.
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 And it shall be for a signe and for a witnes vnto the Lord of hostes in the land of Egypt: for they shall crie vnto the Lord, because of the oppressers, and he shall send them a Sauiour and a great man, and shall deliuer them.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 And the Lord shall be knowen of the Egyptians, and the Egyptians shall knowe the Lord in that day, and doe sacrifice and oblation, and shall vowe vowes vnto the Lord, and performe them.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 So ye Lord shall smite Egypt, he shall smite and heale it: for he shall returne vnto ye Lord, and he shall be intreated of them and shall heale them.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 In that day shall there be a path from Egypt to Asshur, and Asshur shall come into Egypt, and Egypt into Asshur: so the Egyptians shall worship with Asshur.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 In that day shall Israel be the third with Egypt and Asshur, euen a blessing in the middes of the land.
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 For the Lord of hostes shall blesse it, saying, Blessed be my people Egypt and Asshur, the worke of mine hands, and Israel mine inheritance.
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”