< Isaiah 18 >
1 Oh, the lande shadowing with winges, which is beyond the riuers of Ethiopia,
Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 Sending ambassadours by the Sea, euen in vessels of reedes vpon the waters, saying, Go, ye swift messengers, to a nation that is scattered abroade, and spoyled, vnto a terrible people from their beginning euen hitherto: a nation by litle and litle, euen troden vnder foote, whose land the floods haue spoyled.
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Al ye the inhabitants of ye world and dwellers in the earth, shall see when he setteth vp a signe in the mountaines, and when he bloweth the trumpet, ye shall heare.
Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
4 For so the Lord saide vnto me, I will rest and beholde in my tabernacle, as the heate drying vp the rayne, and as a cloude of dewe in the heate of haruest.
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 For afore the haruest when the floure is finished, and the fruite is riping in the floure, then he shall cut downe the branches with hookes, and shall take away, and cut off the boughes:
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 They shall be left together vnto the foules of the mountaines, and to the beastes of the earth: for the foule shall sommer vpon it, and euery beast of the earth shall winter vpon it.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 At that time shall a present be brought vnto the Lord of hostes, (a people that is scattered abroade, and spoyled, and of a terrible people from their beginning hitherto, a nation, by litle and litle euen troden vnder foote, whose land the riuers haue spoyled) to the place of the Name of the Lord of hostes, euen the mount Zion.
Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.