< Isaiah 15 >

1 The burden of Moab. Surely Ar of Moab was destroied, and brought to silece in a night: surely Kir of Moab was destroied, and brought to silence in a night.
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 He shall goe vp to the temple, and to Dibon to the hie places to weepe: for Nebo and for Medeba shall Moab howle: vpon all their heades shalbe baldnesse, and euery beard shauen.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 In their streetes shall they bee gilded with sackecloth: on the toppes of their houses, and in their streetes euery one shall howle, and come downe with weeping.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 And Heshbon shall crie, and Elealeh: their voyce shall bee heard vnto Iahaz: therefore the warriers of Moab shall showt: the soule of euery one shall lament in him selfe.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 Mine heart shall crie for Moab: his fugitiues shall flee vnto Zoar, an heiffer of three yere olde: for they shall goe vp with weeping by the mounting vp of Luhith: and by the way of Horonaim they shall raise vp a crie of destruction.
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 For the waters of Nimrim shall be dried vp: therefore the grasse is withered, the herbes consumed, and there was no greene herbe.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Therefore what euery man hath left, and their substance shall they beare to the brooke of the willowes.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 For the crie went round about the borders of Moab: and the howling thereof vnto Eglaim, and the skriking thereof vnto Beer Elim,
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 Because the waters of Dimon shall be full of blood: for I will bring more vpon Dimon, euen lyons vpon him that escapeth of Moab, and to the remnant of the land.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

< Isaiah 15 >