< Hosea 5 >

1 O ye Priestes, heare this, and hearken ye, O house of Israel, and giue ye eare, O house of the King: for iudgement is towarde you, because you haue bene a snare on Mizpah, and a net spred vpon Tabor.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 Yet they were profounde, to decline to slaughter, though I haue bene a rebuker of them all.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 I knowe Ephraim, and Israel is not hid from me: for nowe, O Ephraim thou art become an harlot, and Israel is defiled.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 They will not giue their mindes to turne vnto their God: for the spirit of fornication is in the middes of them, and they haue not knowen the Lord.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 And the pride of Israel doth testifie to his face: therefore shall Israel and Ephraim fall in their iniquitie: Iudah also shall fall with them.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 They shall goe with their sheepe, and with their bullockes to seeke the Lord: but they shall not finde him: for he hath withdrawne himselfe from them.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 They haue transgressed against the Lord: for they haue begotte strange children: now shall a moneth deuoure them with their portions.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Blowe ye the trumpet in Gibeah, and the shaume in Ramah: crie out at Beth-auen, after thee, O Beniamin.
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Ephraim shall be desolate in the day of rebuke: among the tribes of Israel haue I caused to knowe the trueth.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 The princes of Iudah were like them that remoue the bounde: therefore will I powre out my wrath vpon them like water.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Ephraim is oppressed, and broken in iudgement, because he willingly walked after the commandement.
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 Therefore wil I be vnto Ephraim as a moth, and to the house of Iudah as a rottennesse.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 When Ephraim sawe his sickenes, and Iudah his wound, then went Ephraim vnto Asshur, and sent vnto King Iareb: yet coulde hee not heale you, nor cure you of your wound.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 For I will be vnto Ephraim as a lyon, and as a lyons whelpe to the house of Iudah: I, euen I will spoyle, and goe away: I will take away, and none shall rescue it.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 I will go, and returne to my place, til they acknowledge their fault, and seeke me: in their affliction they will seeke me diligently.
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

< Hosea 5 >