< Hosea 3 >

1 Then said the Lord to me, Goe yet, and loue a woman (beloued of her husband, and was an harlot) according to the loue of the Lord toward the children of Israel: yet they looked to other gods, and loued the wine bottels.
Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 So I bought her to me for fifteene pieces of siluer, and for an homer of barlie and an halfe homer of barlie.
Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
3 And I said vnto her, Thou shalt abide with me many dayes: thou shalt not play the harlot, and thou shalt be to none other man, and I will be so vnto thee.
Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 For the children of Israel shall remaine many dayes without a King and without a prince, and without an offering, and without an image, and without an Ephod and without Teraphim.
Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
5 Afterward shall the children of Israel conuert, and seeke the Lord their God, and Dauid their King, and shall feare the Lord, and his goodnes in the latter dayes.
Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

< Hosea 3 >