< Hosea 2 >

1 Say vnto your brethren, Ammi, and to your sisters, Ruhamah,
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Plead with your mother: plead with her: for she is not my wife, neither am I her husband: but let her take away her fornications out of her sight, and her adulteries from betweene her breasts.
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Lest I strippe her naked, and set her as in the day that shee was borne, and make her as a wildernes, and leaue her like a drie land, and slaie her for thirst.
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 And I wil haue no pitie vpon her children: for they be the children of fornications.
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 For their mother hath plaied the harlot: she that conceiued them, hath done shamefully: for shee said, I will goe after my louers that giue me my bread and my water, my wooll and my flaxe, mine oyle and my drinke.
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Therefore beholde, I will stoope thy way with thornes, and make an hedge, that shee shall not finde her pathes.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 Though shee follow after her louers, yet shall shee not come at them: though shee seeke them, yet shall shee not finde them: then shall she say, I will goe and returne to my first husband: for at that time was I better then nowe.
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 Nowe she did not knowe that I gaue her corne, and wine, and oyle, and multiplied her siluer and golde, which they bestowed vpon Baal.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Therefore wil I returne, and take away my corne in the time thereof, and my wine in the season thereof, and will recouer my wool and my flaxe lent, to couer her shame.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 And now will I discouer her lewdnes in the sight of her louers, and no man shall deliuer her out of mine hand.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 I will also cause all her mirth to cease, her feast daies, her newe moones, and her Sabbathes, and all her solemne feasts.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 And I wil destroy her vines and her figtrees, whereof she hath said, These are my rewards that my louers haue giuen mee: and I will make them as a forest, and the wilde beasts shall eate them.
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 And I wil visit vpon her the daies of Baalim, wherein shee burnt incense to them: and shee decked her selfe with her earings and her iewels, and shee folowed her louers, and forgate me, saith the Lord.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 Therefore beholde, I will allure her, and bring her into the wildernesse, and speake friendly vnto her.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 And I will giue her her vineyardes from thence, and the valley of Achor for the doore of hope, and shee shall sing there as in the daies of her youth, and as in the daies when shee came vp out of the land of Egypt.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 And at that day, sayeth the Lord, thou shalt call me Ishi, and shalt call me no more Baali.
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 For I will take away the names of Baalim out of her mouth, and they shall be no more remembred by their names.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 And in that day wil I make a couenant for them, with the wilde beasts, and with the foules of the heauen, and with that that creepeth vpon the earth: and I will breake the bowe, and the sworde and the battell out of the earth, and will make them to sleepe safely.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 And I wil marry thee vnto me for euer: yea, I will marry thee vnto me in righteousnes, and in iudgement, and in mercy and in compassion.
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 I will euen marry thee vnto me in faithfulnes, and thou shalt knowe the Lord.
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 And in that day I wil heare, saith the Lord, I will euen heare the heauens, and they shall heare the earth,
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 And the earth shall heare the corne, and the wine, and the oyle, and they shall heare Izreel.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 And I will sowe her vnto me in the earth, and I will haue mercie vpon her, that was not pitied, and I will say to them which were not my people, Thou art my people. And they shall say, Thou art my God.
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Hosea 2 >