< Hosea 10 >
1 Israel is a emptie vine, yet hath it brought foorth fruite vnto it selfe, and according to the multitude of the fruite thereof he hath increased the altars: according to the goodnesse of their lande they haue made faire images.
Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 Their heart is deuided: nowe shall they be founde faultie: he shall breake downe their altars: he shall destroy their images.
Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 For now they shall say, We haue no King because we feared not the Lord: and what should a King doe to vs?
Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 They haue spoken woordes, swearing falsly in making a couenant: thus iudgement groweth as wormewoode in the furrowes of the fielde.
Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 The inhabitants of Samaria shall feare because of the calfe of Beth-auen: for the people thereof shall mourne ouer it, and the Chemarims thereof, that reioyced on it for the glorie thereof, because it is departed from it.
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 It shall bee also brought to Asshur, for a present vnto King Iareb: Ephraim shall receiue shame, and Israel shall be ashamed of his owne counsell.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 Of Samaria, the King thereof is destroyed as the some vpon the water.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 The hie places also of Auen shall be destroied, euen the sinne of Israel: the thorne and the thistle shall growe vpon their altars, and they shall say to the mountaines, Couer vs, and to the hils, Fall vpon vs.
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 O Israel, thou hast sinned from the daies of Gibeah: there they stoode: the battell in Gibeah against the children of iniquitie did not touch them.
“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
10 It is my desire that I should chastice them, and the people shall be gathered against them, when they shall gather themselues in their two furrowes.
Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 And Ephraim is as an heifer vsed to delite in threshing: but I will passe by her faire necke: I will make Ephraim to ride: Iudah shall plowe, and Iaakob shall breake his cloddes.
Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Sowe to your selues in righteousnes: reape after the measure of mercy: breake vp your fallowe grounde: for it is time to seeke the Lord, till he come and raine righteousnesse vpon you.
Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 But you haue plowed wickednesse: ye haue reaped iniquitie: you haue eaten the fruite of lies: because thou didest trust in thine owne waies, and in the multitude of thy strong men,
Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 Therefore shall a tumult arise among thy people, and all thy munitions shall be destroyed, as Shalman destroyed Beth-arbell in the daie of battell: the mother with the children was dashed in pieces.
phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 So shall Beth-el doe vnto you, because of your malicious wickednes: in a morning shall the King of Israel be destroied.
Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.