< Hebrews 1 >

1 At sundry times and in diuers maners God spake in the olde time to our fathers by the Prophetes:
Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri.
2 in these last dayes hee hath spoken vnto vs by his Sonne, Whom he hath made heire of al things, by whome also he made the worldes, (aiōn g165)
Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. (aiōn g165)
3 Who being the brightnes of the glory, and the ingraued forme of his person, and bearing vp all things by his mightie worde, hath by himselfe purged our sinnes, and sitteth at the right hand of the Maiestie in the highest places,
Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero.
4 And is made so much more excellent then the Angels, in as much as hee hath obteined a more excellent Name then they.
Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.
5 For vnto which of the Angels saide he at any time, Thou art my Sonne, this day begate I thee? and againe, I will be his Father, and he shalbe my Sonne?
Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati, “Iwe ndiwe mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.” Kapena kunenanso kuti, “Ine ndidzakhala abambo ake; iye adzakhala mwana wanga.”
6 And againe, when he bringeth in his first begotten Sonne into the worlde, hee saith, And let all the Angels of God worship him.
Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati, “Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”
7 And of the Angels he saith, He maketh the spirites his messengers, and his ministers a flame of fire.
Iye ponena za angelo akuti, “Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo, amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”
8 But vnto the Sonne he saith, O God, thy throne is for euer and euer: the scepter of thy kingdome is a scepter of righteousnes. (aiōn g165)
Koma za Mwana wake akuti, “Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya, ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu. (aiōn g165)
9 Thou hast loued righteousnes and hated iniquitie. Wherefore God, eue thy God, hath anointed thee with the oyle of gladnes aboue thy fellowes.
Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”
10 And, Thou, Lord, in the beginning hast established the earth, and the heauens are the workes of thine handes.
Mulungu akutinso, “Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi; ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
11 They shall perish, but thou doest remaine: and they all shall waxe olde as doeth a garment.
Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire. Izo zidzatha ngati zovala.
12 And as a vesture shalt thou folde them vp, and they shall be changed: but thou art the same, and thy yeeres shall not faile.
Mudzazipindapinda ngati chofunda; ndipo zidzasinthidwa ngati chovala. Koma Inu simudzasintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.”
13 Vnto which also of the Angels saide he at any time, Sit at my right hand, til I make thine enemies thy footestoole?
Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti, “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditapanga adani ako kukhale chopondapo mapazi ako.”
14 Are they not al ministring spirits, sent forth to minister, for their sakes which shalbe heires of saluation?
Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

< Hebrews 1 >