< Genesis 6 >
1 So when men began to be multiplied vpon the earth, and there were daughters borne vnto them,
Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi,
2 Then the sonnes of God sawe the daughters of men that they were faire, and they tooke them wiues of all that they liked.
ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha.
3 Therefore the Lord saide, My Spirit shall not alway striue with man, because he is but flesh, and his dayes shalbe an hundreth and twentie yeeres.
Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”
4 There were gyants in the earth in those dayes: yea, and after that the sonnes of God came vnto the daughters of men, and they had borne them children, these were mightie men, which in olde time were men of renoume.
Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.
5 When the Lord sawe that the wickednesse of man was great in the earth, and all the imaginations of the thoughtes of his heart were onely euill continually,
Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha,
6 Then it repented ye Lord, that he had made man in the earth, and he was sorie in his heart.
Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima.
7 Therefore ye Lord said, I will destroy from the earth the man, whom I haue created, from man to beast, to the creeping thing, and to the foule of the heauen: for I repent that I haue made them.
Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.”
8 But Noah found grace in the eyes of the Lord.
Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.
9 These are the generations of Noah. Noah was a iust and vpright man in his time: and Noah walked with God.
Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
10 And Noah begate three sonnes, Shem, Ham and Iapheth.
Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.
11 The earth also was corrupt before God: for the earth was filled with crueltie.
Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu.
12 Then God looked vpon the earth, and beholde, it was corrupt: for all flesh had corrupt his way vpon the earth.
Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi.
13 And God said vnto Noah, An ende of all flesh is come before me: for the earth is filled with crueltie through them: and beholde, I wil destroy them with the earth.
Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko.
14 Make thee an Arke of pine trees: thou shalt make cabines in the Arke, and shalt pitch it within and without with pitch.
Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja.
15 And thus shalt thou make it: The length of the Arke shalbe three hundreth cubites, the breadth of it fiftie cubites, and the height of it thirtie cubites.
Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake.
16 A windowe shalt thou make in the Arke, and in a cubite shalt thou finish it aboue, and the doore of the Arke shalt thou set in the side thereof: thou shalt make it with the lowe, seconde and third roume.
Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba.
17 And I, beholde, I will bring a flood of waters vpon the earth to destroy all flesh, wherein is the breath of life vnder the heauen: all that is in the earth shall perish.
Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa.
18 But with thee will I establish my couenant, and thou shalt goe into the Arke, thou, and thy sonnes, and thy wife, and thy sonnes wiues with thee.
Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho.
19 And of euery liuing thing, of all flesh two of euery sort shalt thou cause to come into the Arke, to keepe them aliue with thee: they shalbe male and female.
Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe.
20 Of the foules, after their kinde, and of the cattell after their kind, of euery creeping thing of the earth after his kinde, two of euery sort shall come vnto thee, that thou mayest keepe them aliue.
Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo.
21 And take thou with thee of all meate that is eaten: and thou shalt gather it to thee, that it may be meate for thee and for them.
Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”
22 Noah therefore did according vnto all, that God commanded him: euen so did he.
Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.