< Genesis 44 >

1 Afterward he commanded his steward, saying, Fill the mens sackes with foode, as much as they can carry, and put euery mans money in his sackes mouth.
Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
2 And put my cup, I meane the siluer cup, in the sackes mouth of the yongest, and his corne money. And he did according to the commandement that Ioseph gaue him.
Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
3 And in the morning the men were sent away, they, and their asses.
Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
4 And when they went out of the citie not farre off, Ioseph sayd to his stewarde, Vp, follow after the men: and when thou doest ouertake them, say vnto them, Wherefore haue ye rewarded euill for good?
Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
5 Is that not the cuppe, wherein my Lord drinketh? and in the which he doeth deuine and prophecie? ye haue done euill in so doing.
Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
6 And when he ouertooke them, he sayde those wordes vnto them.
Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
7 And they answered him, Wherefore sayeth my lorde such wordes? God forbid that thy seruants should do such a thing.
Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
8 Behold, the money which we found in our sackes mouthes, wee brought againe to thee out of the land of Canaan: how then should we steale out of thy lordes house siluer or golde?
Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
9 With whomesoeuer of thy seruants it bee found, let him dye, and we also will be my lordes bondmen.
Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
10 And he said, Now then let it be according vnto your wordes: he with whome it is found, shall be my seruant, and ye shalbe blamelesse.
Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
11 Then at once euery man tooke downe his sacke to the grounde, and euery one opened his sacke.
Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
12 And he searched, and began at the eldest and left at the yongest: and the cuppe was found in Beniamins sacke.
Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
13 Then they rent their clothes, and laded euery man his asse, and went againe into the citie.
Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
14 So Iudah and his brethren came to Iosephs house (for he was yet there) and they fel before him on the ground.
Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
15 Then Ioseph sayd vnto them, What acte is this, which ye haue done? know ye not that such a man as I, can deuine and prophecie?
Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
16 Then sayd Iudah, What shall we say vnto my lord? what shall we speake? and howe can we iustifie our selues? God hath found out the wickednesse of thy seruants: beholde, we are seruants to my Lord, both wee, and he, with whome the cuppe is founde.
Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
17 But he answered, God forbid, that I should doe so, but the man, with whome the cuppe is founde, he shalbe my seruant, and go ye in peace vnto your father.
Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
18 Then Iudah drewe neere vnto him, and sayde, O my Lord, let thy seruant nowe speake a worde in my lordes eares, and let not thy wrath be kindled against thy seruant: for thou art euen as Pharaoh.
Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
19 My Lord asked his seruants, saying, Haue ye a father, or a brother?
Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
20 And we answered my Lord, We haue a father that is olde, and a young childe, which he begate in his age: and his brother is dead, and he alone is left of his mother, and his father loueth him.
Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
21 Now thou saidest vnto thy seruants, Bring him vnto me, that I may set mine eye vpon him.
“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
22 And we answered my lord, The childe can not depart from his father: for if he leaue his father, his father would die.
Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
23 Then saydest thou vnto thy seruants, Except your yonger brother come downe with you, looke in my face no more.
Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
24 So when we came vnto thy seruant our father, and shewed him what my lord had sayd,
Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
25 And our father sayde vnto vs, Goe againe, bye vs a litle foode,
“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
26 Then we answered, We can not go downe: but if our yongest brother go with vs, then will we go downe: for we may not see the mans face, except our yongest brother be with vs.
Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
27 Then thy seruant my father sayde vnto vs, Ye knowe that my wife bare me two sonnes,
“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
28 And the one went out from me, and I said, Of a suretie he is torne in pieces, and I sawe him not since.
Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
29 Nowe yee take this also away from me: if death take him, then yee shall bring my graye head in sorowe to the graue. (Sheol h7585)
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
30 Nowe therefore, when I come to thy seruant my father, and the childe be not with vs (seeing that his life dependeth on the childes life)
“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
31 Then when hee shall see that the childe is not come, he will die: so shall thy seruants bring the graye head of thy seruant our father with sorowe to the graue. (Sheol h7585)
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
32 Doubtlesse thy seruant became suertie for the childe to my father, and said, If I bring him not vnto thee againe, then I will beare the blame vnto my father for euer.
Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
33 Nowe therefore, I pray thee, let me thy seruant bide for the childe, as a seruant to my Lord, and let the childe go vp with his brethren.
“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
34 For how can I go vp to my father, if the childe be not with me, vnlesse I woulde see the euil that shall come on my father?
Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

< Genesis 44 >