< Genesis 33 >

1 And as Iaakob lift vp his eyes, and looked, behold, Esau came, and with him foure hundreth men: and he deuided the children to Leah, and to Rahel, and to the two maides.
Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja.
2 And he put the maides, and their children formost, and Leah, and her children after, and Rahel, and Ioseph hindermost.
Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe.
3 So he went before them and bowed him selfe to the ground seuen times, vntill he came neere to his brother.
Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.
4 Then Esau ranne to meete him, and embraced him, and fell on his necke, and kissed him, and they wept.
Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira.
5 And he lift vp his eyes, and sawe the women, and the children, and saide, Who are these with thee? And he answered, They are ye childre whome God of his grace hath giuen thy seruant.
Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?” Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”
6 Then came the maides neere, they, and their children, and bowed themselues.
Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi.
7 Leah also with her children came neere and made obeysance: and after Ioseph and Rahel drew neere, and did reuerence.
Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.
8 Then he said, What meanest thou by all this droue, which I met? Who answered, I haue sent it, that I may finde fauour in the sight of my lorde:
Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?” Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”
9 And Esau said, I haue ynough, my brother: keepe that thou hast to thy selfe.
Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”
10 But Iaakob answered, Nay, I pray thee: if I haue found grace nowe in thy sight, then receiue my present at mine hande: for I haue seene thy face, as though I had seene the face of God, because thou hast accepted me.
Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu.
11 I pray thee take my blessing, that is brought thee: for God hath had mercie on me, and therefore I haue all things: so he compelled him, and he tooke it.
Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.
12 And he saide, Let vs take our iourney and go, and I will goe before thee.
Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”
13 Then he answered him, My lord knoweth, that the children are tender, and the ewes and kine with yong vnder mine hande: and if they should ouerdriue them one day, all the flocke would die.
Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.
14 Let now my lord go before his seruant, and I will driue softly, according to ye pase of ye cattel, which is before me, and as the children be able to endure, vntill I come to my lord vnto Seir.
Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”
15 Then Esau said, I will leaue then some of my folke with thee. And he answered, what needeth this? let me finde grace in the sight of my lorde.
Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.” Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”
16 So Esau returned, and went his way that same day vnto Seir.
Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri.
17 And Iaakob went forwarde towarde Succoth, and built him an house, and made boothes for his cattell: therefore he called the name of the place Succoth.
Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.
18 Afterward, Iaakob came safe to Sheche a citie, which is in the lande of Canaan, when he came from Padan Aram, and pitched before the citie.
Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo.
19 And there he bought a parcell of ground, where hee pitched his tent, at the hande of the sonnes of Hamor Shechems father, for an hundreth pieces of money.
Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva.
20 And he set vp there an altar, and called it, The mightie God of Israel.
Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.

< Genesis 33 >