< Genesis 32 >

1 Nowe Iaakob went forth on his iourney and the Angels of God met him.
Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
2 And when Iaakob saw them, he said, This is Gods hoste, and called the name of the same place Mahanaim.
Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
3 Then Iaakob sent messengers before him to Esau his brother, vnto the land of Seir into the countrey of Edom:
Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
4 To whom he gaue commandement, saying, Thus shall ye speake to my lorde Esau: thy seruant Iaakob sayeth thus, I haue bene a stranger with Laban, and taried vnto this time.
Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
5 I haue beeues also and Asses, sheepe, and men seruantes, and women seruantes, and haue sent to shew my lord, that I may find grace in thy sight.
Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
6 So ye messengers came againe to Iaakob, saying, We came vnto thy brother Esau, and hee also commeth against thee and foure hundreth men with him.
Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
7 Then Iaakob was greatly afraid, and was sore troubled, and deuided the people that was with him, and the sheepe, and the beeues, and the camels into two companies.
Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
8 For he said, If Esau come to ye one company and smite it, the other companie shall escape.
Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
9 Moreouer Iaakob said, O God of my father Abraham, and God of my father Izhak: Lord, which saydest vnto me, Returne vnto thy coutrey and to thy kinred, and I will do thee good,
Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
10 I am not worthy of the least of all the mercies, and al the trueth, which thou hast shewed vnto thy seruant: for with my staffe came I ouer this Iorden, and now haue I gotte two bads.
Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
11 I pray thee, Deliuer me from the hande of my brother, from the hande of Esau: for I feare him, least he will come and smite me, and the mother vpon the children.
Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
12 For thou saydest; I will surely doe thee good, and make thy seede as the sande of the sea, which can not be nombred for multitude.
Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
13 And he taryed there the same night, and tooke of that which came to had, a present for Esau his brother:
Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
14 Two hundreth shee goates and twenty hee goates, two hundreth ewes and twentie rammes:
Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
15 Thirtie mylche camels with their coltes, fourtie kine, and ten bullockes, twentie she asses and ten foles.
ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
16 So he deliuered them into the hande of his seruants, euery droue by themselues, and saide vnto his seruants, Passe before me, and put a space betweene droue and droue.
Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
17 And he commanded the formost, saying, If Esau my brother meete thee, and aske thee, saying, Whose seruant art thou? And whither goest thou? And whose are these before thee?
Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
18 Then thou shalt say, They be thy seruant Iaakobs: it is a present sent vnto my lord Esau: and beholde, he him selfe also is behinde vs.
Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
19 So likewise commanded he the seconde and the thirde, and all that followed the droues, saying, After this maner, ye shall speake vnto Esau, when ye finde him.
Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
20 And ye shall say moreouer, Beholde, thy seruant Iaakob commeth after vs (for he thought, I will appease his wrath with the present that goeth before me, and afterwarde I will see his face: it may be that he will accept me.)
Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
21 So went the present before him: but he taried that night with the companie.
Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
22 And he rose vp the same night, and tooke his two wiues, and his two maides, and his eleuen children, and went ouer the forde Iabbok.
Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
23 And he tooke them, and sent them ouer the riuer, and sent ouer that he had.
Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
24 Now when Iaakob was left him selfe alone, there wrestled a man with him vnto the breaking of the day.
Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
25 And he sawe that he could not preuaile against him: therefore he touched the holowe of his thigh, and the holowe of Iaakobs thigh was loosed, as he wrestled with him.
Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
26 And he saide, Let me goe, for the morning appeareth. Who answered, I will not let thee go except thou blesse me.
Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
27 Then said he vnto him, What is thy name? And he said, Iaakob.
Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
28 Then said he, Thy name shalbe called Iaakob no more, but Israel: because thou hast had power with God, thou shalt also preuaile with men.
Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
29 Then Iaakob demaded, saying, Tell me, I pray thee, thy name. And he said, Wherefore now doest thou aske my name? and he blessed him there
Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
30 And Iaakob called the name of the place, Peniel: for, saide he, I haue seene God face to face, and my life is preserued.
Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
31 And the sunne rose vp to him as he passed Peniel, and he halted vpon his thigh.
Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
32 Therefore the children of Israel eate not of the sinewe that shranke in the hollowe of the thigh, vnto this day: because he touched the sinew that shranke in the holow of Iaakobs thigh.
Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.

< Genesis 32 >