< Genesis 29 >
1 Then Iaakob lift vp his feete and came into the East countrey.
Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
2 And as he looked about, behold there was a well in the field, and lo, three flocks of sheepe lay thereby (for at that well were the flockes watered) and there was a great stone vpon the welles mouth.
Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
3 And thither were all the flockes gathered, and they rolled the stone from the welles mouth, and watered the sheepe, and put the stone againe vpon the welles mouth in his place.
Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
4 And Iaakob sayde vnto them, My brethren, whence be ye? And they answered, We are of Haran.
Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
5 Then he sayd vnto them, Know ye Laban the sonne of Nahor? Who said, We know him.
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
6 Againe he sayd vnto them, Is he in good health? And they answered, He is in good health, and beholde, his daughter Rahel commeth with the sheepe.
Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
7 Then he sayd, Lo, it is yet hie day, neither is it time that the cattell shoulde be gathered together: water ye the sheepe and go feede them.
Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
8 But they sayde, We may not vntill all the flocks be brought together, and till men rolle the stone from the welles mouth, that we may water the sheepe.
Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
9 While he talked with them, Rahel also came with her fathers sheepe, for she kept them.
Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
10 And assoone as Iaakob saw Rahel ye daughter of Laban his mothers brother, and the sheepe of Laban his mothers brother, then came Iaakob neere, and rolled the stone from the welles mouth, and watered ye flocke of Laban his mothers brother.
Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
11 And Iaakob kissed Rahel, and lift vp his voyce and wept.
Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
12 (For Iaakob tolde Rahel, that he was her fathers brother, and that he was Rebekahs sonne) then she ranne and tolde her father.
Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
13 And when Laban heard tell of Iaakob his sisters sonne, he ranne to meete him, and embraced him and kissed him, and brought him to his house: and he tolde Laban all these things.
Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
14 To whome Laban sayd, Well, thou art my bone and my flesh. and he abode with him the space of a moneth.
Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
15 For Laban sayde vnto Iaakob, Though thou be my brother, shouldest thou therfore serue me for nought? tell me, what shalbe thy wages?
Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
16 Now Laban had two daughters, the elder called Leah, and the yonger called Rahel.
Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
17 And Leah was tender eyed, but Rahel was beautifull and faire.
Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
18 And Iaakob loued Rahel, and sayde, I will serue thee seuen yeeres for Rahel thy yonger daughter.
Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
19 Then Laban answered, It is better that I giue her thee, then that I should giue her to another man: abide with me.
Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
20 And Iaakob serued seuen yeres for Rahel, and they seemed vnto him but a few dayes, because he loued her.
Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
21 Then Iaakob sayde to Laban, Giue me my wife, that I may goe in to her: for my terme is ended.
Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
22 Wherefore Laban gathered together all the men of the place, and made a feast.
Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
23 But whe the euening was come, he tooke Leah his daughter and brought her to him, and he went in vnto her.
Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
24 And Laban gaue his mayde Zilpah to his daughter Leah, to be her seruant.
Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
25 But when the morning was come, behold, it was Leah. Then sayde he to Laban, Wherefore hast thou done thus to mee? did not I serue thee for Rahel? wherfore then hast thou beguiled me?
Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
26 And Laban answered, It is not the maner of this place, to giue the yonger before the elder.
Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
27 Fulfill seuen yeeres for her, and we wil also giue thee this for the seruice, which thou shalt serue me yet seuen yeeres more.
Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
28 Then Iaakob did so, and fulfilled her seuen yeeres, so he gaue him Rahel his daughter to be his wife.
Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
29 Laban also gaue to Rahel his daughter Bilhah his mayde to be her seruant.
Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
30 So entred he in to Rahel also, and loued also Rahel more then Leah, and serued him yet seuen yeeres more.
Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
31 When the Lord saw that Leah was despised, he made her fruitful: but Rahel was barren.
Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
32 And Leah conceiued and bare a sonne, and she called his name Reuben: for she said, Because the Lord hath looked vpon my tribulation, now therefore mine husband will loue me.
Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
33 And she conceiued againe and bare a sonne, and sayde, Because the Lord heard that I was hated, he hath therefore giuen me this sonne also, and she called his name Simeon.
Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
34 And she conceiued againe and bare a sonne, and said, Now at this time wil my husband keepe mee company, because I haue borne him three sonnes: therefore was his name called Leui.
Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
35 Moreouer shee conceiued againe and bare a sonne, saying, Nowe will I prayse the Lord: therefore shee called his name Iudah, and left bearing.
Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.