< Genesis 23 >
1 When Sarah was an hundreth twentie and seuen yeere olde (so long liued she).
Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
2 Then Sarah dyed in Kiriath-arba: the same is Hebron in the land of Canaan. and Abraham came to mourne for Sarah and to weepe for her.
Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
3 Then Abraham rose vp from the sight of his corps, and talked with the Hittites, saying,
Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
4 I am a stranger, and a forreiner among you, giue me a possession of buriall with you, that I may burie my dead out of my sight.
“Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
5 Then the Hittites answered Abraham, saying vnto him,
Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
6 Heare vs, my lorde: thou art a prince of God among vs: in the chiefest of our sepulchres bury thy dead: none of vs shall forbid thee his sepulchre, but thou mayest bury thy dead therein.
“Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
7 Then Abraham stoode vp, and bowed him selfe before the people of the land of the Hittites.
Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
8 And he communed with them, saying, If it be your minde, that I shall bury my dead out of my sight, heare me, and intreate for me to Ephron the sonne of Zohar,
nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
9 That he would giue me ye caue of Machpelah, which he hath in the ende of his field: that he would giue it me for as much money as it is worth, for a possession to bury in among you.
kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
10 (For Ephron dwelt among the Hittites) Then Ephron the Hittite answered Abraham in the audience of all the Hittites that went in at the gates of his citie, saying,
Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
11 No, my Lord, heare me: the fielde giue I thee, and the caue, that therein is, I giue it thee: euen in the presence of the sonnes of my people giue I it thee, to bury thy dead.
nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
12 Then Abraham bowed himselfe before the people of the land,
Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
13 And spake vnto Ephron in the audience of the people of the countrey, saying, Seeing thou wilt giue it, I pray thee, heare me, I will giue the price of the fielde: receiue it of me, and I will bury my dead there.
ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
14 Ephron then answered Abraham, saying vnto him,
Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
15 My lord, hearken vnto me: ye land is worth foure hundreth shekels of siluer: what is that betweene me and thee? bury therefore thy dead.
“Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
16 So Abraham hearkened vnto Ephron, and Abraham weyed to Ephron the siluer, which he had named, in the audience of the Hittites, euen foure hundreth siluer shekels of currant money among marchants.
Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
17 So the fielde of Ephron which was in Machpelah, and ouer against Mamre, euen the field and the caue that was therein, and all the trees that were in the fielde, which were in all the borders round about, was made sure
Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
18 Vnto Abraham for a possession, in ye sight of the Hittites, euen of all that went in at the gates of his citie.
kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
19 And after this, Abraham buried Sarah his wife in the caue of the fielde of Machpelah ouer against Mamre: the same is Hebron in the land of Canaan.
Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
20 Thus the fielde and the caue, that is therein, was made sure vnto Abraham for a possession of buriall by the Hittites.
Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.