< Genesis 22 >

1 And after these things God did proue Abraham, and said vnto him, Abraham. Who answered, Here am I.
Nthawi ina zitatha izi, Mulungu anamuyesa Abrahamu. Iye anati, “Abrahamu!” Ndipo iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
2 And he said, Take nowe thine onely sonne Izhak whom thou louest, and get thee vnto the land of Moriah, and offer him there for a burnt offering vpon one of the mountaines, which I will shewe thee.
Ndipo Mulungu anati, “Tenga Isake, mwana wako yekhayo amene umamukonda ndi kupita naye ku dziko la Moriya. Ukamupereke iye ngati nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri a kumeneko limene ndidzakuwuza.”
3 Then Abraham rose vp early in the morning, and sadled his asse, and tooke two of his seruants with him, and Izhak his sonne, and cloue wood for the burnt offering, and rose vp and went to the place, which God had tolde him.
Abrahamu anadzuka mmamawa wake namangirira chokhalira pa bulu. Atadula nkhuni zokwanira zowotchera nsembe yopsereza, Abrahamu, antchito ake awiri pamodzi ndi Isake ananyamuka kupita kumalo kumene Mulungu anamuwuza Abrahamu.
4 Then the third day Abraham lift vp his eyes, and sawe the place afarre off,
Pa tsiku lachitatu, Abrahamu anakweza maso ake ndipo anaona malowo chapatali.
5 And said vnto his seruants, Abide you here with the asse: for I and the childe will go yonder and worship, and come againe vnto you.
Ndipo Abrahamu anati kwa antchito ake aja, “Bakhalani pano ndi buluyu. Ine ndi mnyamatayu tipita uko kukapemphera, koma tibweranso.”
6 Then Abraham tooke the wood of the burnt offering, and layed it vpon Izhak his sonne, and he tooke the fire in his hand, and the knife: and they went both together.
Abrahamu anatenga nkhuni za nsembe yopsereza zija namusenzetsa mwana wake Isake, ndipo iye mwini anatenga moto ndi mpeni. Pamene awiriwo amayendera pamodzi,
7 Then spake Izhak vnto Abraham his father, and said, My father. And he answered, Here am I, my sonne. And he said, Behold the fire and the wood, but where is the lambe for ye burnt offring?
Isake anati kwa abambo ake Abrahamu, “Abambo?” Abrahamu anayankha, “Ee mwana wanga.” Isake anafunsa, “Moto ndi nkhuni zilipo, koma nanga mwana wankhosa wa nsembe yopsereza ali kuti?”
8 Then Abraham answered, My sonne, God will prouide him a lambe for a burnt offering: so they went both together.
Abrahamu anayankha, “Mwana wanga, Mulungu adzipezera yekha mwana wankhosa wa nsembe yopsereza.” Ndipo awiriwo anapitiriza ulendo.
9 And when they came to the place which God had shewed him, Abraham builded an altar there, and couched ye wood, and bound Izhak his sonne and laid him on the altar vpon the wood.
Atafika pamalo pamene Mulungu anamuwuza paja, Abrahamu anamangapo guwa lansembe nayika nkhuni pamwamba pa guwapo. Kenaka anamumanga mwana wake Isake namugoneka paguwapo, pamwamba pa nkhuni paja.
10 And Abraham stretching forth his hand, tooke the knife to kill his sonne.
Kenaka Abrahamu anatambasula dzanja lake natenga mpeni kuti aphe mwana wake.
11 But the Angel of the Lord called vnto him from heauen, saying, Abraham, Abraham. And he answered, Here am I.
Koma mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba nati, “Abrahamu! Abrahamu!” Iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
12 Then he said, Lay not thine hand vpon the childe, neither doe any thing vnto him: for now I know that thou fearest God, seeing for my sake thou hast not spared thine onely sonne.
Mngeloyo anati, “Usatambasulire mwanayo dzanja lako kuti umuphe, pakuti tsopano ndadziwa kuti iwe umaopa Mulungu. Iwe sunandimane mwana wako mmodzi yekhayo.”
13 And Abraham lifting vp his eyes, looked: and behold, there was a ramme behind him caught by the hornes in a bush. then Abraham went and tooke the ramme, and offered him vp for a burnt offering in the steade of his sonne.
Abrahamu anatukula maso ake ndipo anaona nkhosa yamphongo itakoledwa ndi nyanga zake mu ziyangoyango. Iye anapita nakatenga nkhosa ija ndikuyipha ngati nsembe yopsereza mʼmalo mwa mwana wake.
14 And Abraham called the name of that place, Iehouah-ijreh. as it is said this day, In the mount will the Lord be seene.
Choncho Abrahamu anatcha malo amenewa kuti Yehova-Yire (Wopereka). Ndipo mpaka lero amatchula malowo kuti ndi “Pa phiri la Yehova wopereka.”
15 And the Angel of the Lord cryed vnto Abraham from heauen the second time,
Mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba kachiwiri
16 And saide, By my selfe haue I sworne (saith ye Lord) because thou hast done this thing, and hast not spared thine onely sonne,
ndipo anati, “Ndikulumbira mwa Ine ndekha kuti popeza wachita zimenezi, wosandikaniza mwana wako mmodzi yekhayu,
17 Therefore will I surely blesse thee, and will greatly multiplie thy seede, as the starres of the heauen, and as the sand which is vpon the sea shore, and thy seede shall possesse the gate of his enemies.
ndidzakudalitsa ndithu ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati nyenyezi zamlengalenga komanso ngati mchenga wa mʼmphepete mwa nyanja. Zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo,
18 And in thy seede shall all the nations of the earth be blessed, because thou hast obeyed my voyce.
ndipo kudzera mwa chidzukulu chako, mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi idzadalitsika, chifukwa iwe wandimvera.”
19 Then turned Abraham againe vnto his seruants, and they rose vp and went together to Beer-sheba: and Abraham dwelt at Beer-sheba.
Kenaka Abrahamu anabwerera kumene anasiya antchito ake kuja nanyamukira nawo pamodzi kupita ku Beeriseba. Ndipo Abrahamu anakhala ku Beeriseba.
20 And after these things one tolde Abraham, saying, Beholde Milcah, she hath also borne children vnto thy brother Nahor:
Patapita nthawi, Abrahamu anamva kuti, “Milika nayenso anaberekera Nahori, mʼbale wake ana.
21 To wit, Vz his eldest sonne, and Buz his brother, and Kemuel the father of Aram,
Woyamba anali Huzi ndipo kenaka mʼbale wake Buzi. Anaberekanso Kemueli, amene anali abambo ake a Aramu.
22 And Chesed and Hazo, and Pildash, and Iidlaph, and Bethuel.
Ana ena ndi Kesede Hazo, Pilidasi, Yidilafi ndi Betueli.”
23 And Bethuel begate Rebekah: these eight did Milcah beare to Nahor Abrahams brother.
Betueli anabereka Rebeka. Milika anaberekera Nahori, mʼbale wake wa Abrahamu, ana aamuna asanu ndi atatu amenewa.
24 And his concubine called Reumah, she bare also Tebah, and Gahan, and Thahash and Maachah.
Mkazi wake wachiwiri, dzina lake Reuma, anamubaliranso Nahori ana awa: Teba, Gahamu, Tahasi ndi Maaka.

< Genesis 22 >