< Ezekiel 9 >
1 He cryed also with a loude voyce in mine eares, saying, The visitations of the citie draw neere, and euery man hath a weapon in his hande to destroy it.
Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
2 And beholde, sixe men came by the way of the hie gate, which lieth towarde the North, and euery man a weapon in his hande to destroy it: and one man among them was clothed with linen, with a writers ynkhorne by his side, and they went in and stoode beside the brasen altar.
Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
3 And the glorie of the God of Israel was gone vp from ye Cherub, whereupon he was and stoode on the doore of the house, and he called to the man clothed with linnen, which had the writers ynkhorne by his side.
Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
4 And the Lord said vnto him, Goe through the middes of the citie, euen through the middes of Ierusalem and set a marke vpon the foreheads of them that mourne, and cry for all the abominations that be done in the middes thereof.
ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
5 And to the other he said, that I might heare, Goe ye after him through the citie, and smite: let your eye spare none, neither haue pitie.
Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
6 Destroy vtterly the old, and the yong, and the maides, and the children, and the women, but touch no man, vpon whome is the marke, and begin at my Sanctuarie. Then they began at the Ancient men, which were before the house.
Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
7 And he sayde vnto them, Defile the house, and fill the courtes with the slaine, then goe foorth: and they went out, and slewe them in the citie.
Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
8 Nowe when they had slaine them, and I had escaped, I fell downe vpon my face, and cryed, saying, Ah Lord God, wilt thou destroy all the residue of Israel, in powring out thy wrath vpon Ierusalem?
Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
9 Then saide he vnto me, The iniquitie of the house of Israel, and Iudah is exceeding great, so that the lande is full of blood, and the citie full of corrupt iudgement: for they say, The Lord hath forsaken the earth, and the Lord seeth vs not.
Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
10 As touching me also, mine eye shall not spare them, neither will I haue pitie, but will recompence their wayes vpon their heades.
Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
11 And beholde, the man clothed with linen which had the ynkhorne by his side, made report, and saide, Lord, I haue done as thou hast commanded me.
Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”