< Ezekiel 45 >

1 Moreover when yee shall deuide the land for inheritance, ye shall offer an oblation vnto the Lord an holy portion of the land, fiue and twentie thousand reedes long, and ten thousand broad: this shalbe holy in all the borders thereof round about.
“‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
2 Of this there shalbe for the Sanctuarie fiue hundreth in length with fiue hundreth in breadth, all square round about, and fiftie cubites rounde about for the suburbes thereof.
Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
3 And of this measure shalt thou measure the length of fiue and twentie thousande, and the breadth of tenne thousande: and in it shalbe the Sanctuarie, and the most holy place.
Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
4 The holy portion of the lande shalbe the Priests, which minister in the Sanctuarie, which came neere to serue the Lord: and it shalbe a place for their houses, and an holy place for the Sanctuarie.
Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
5 And in the fiue and twentie thousande of length, and the ten thousand of breadth shall the Leuites that minister in the house, haue their possession for twentie chambers.
Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
6 Also ye shall appoynt the possession of the citie, fiue thousand broad, and fiue and twentie thousand log ouer against the oblation of ye holy portion: it shalbe for the whole house of Israel.
“‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
7 And a portion shalbe for the prince on ye one side, and on that side of the oblation of the holy portion, and of the possession of the citie, euen before the oblation of the holy portion, and before the possession of the citie from the West corner Westward, and from the East corner Eastward, and the length shalbe by one of the portions from the West border vnto the East border.
“‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
8 In this lande shalbe his possession in Israel: and my princes shall no more oppresse my people, and the rest of the land shall they giue to ye house of Israel, according to their tribes.
Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
9 Thus saith the Lord God, Let it suffice you, O princes of Israel: leaue off crueltie and oppression, and execute iudgment and iustice: take away your exactions from my people, sayth the Lord God.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
10 Ye shall haue iust balances, and a true Ephah, and a true Bath.
Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
11 The Ephah and the Bath shalbe equall: a Bath shall conteyne the tenth part of an Homer, and an Ephah the tenth part of an Homer: the equalitie thereof shalbe after the Homer.
Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
12 And the shekel shalbe twentie gerahs, and twentie shekels, and fiue and twentie shekels and fifteene shekels shalbe your Maneh.
Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
13 This is the oblation that ye shall offer, ye sixt part of an Ephah of an Homer of wheat, and ye shall giue the sixt part of an Ephah of an Homer of barley.
“‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
14 Concerning ye ordinance of the oyle, euen of the Bath of oyle, ye shall offer the tenth part of a Bath out of ye Cor (ten Baths are an Homer: for ten Baths fill an Homer)
Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
15 And one lambe of two hundreth sheepe out of ye fat pastures of Israel for a meat offring, and for a burnt offring and for peace offrings, to make reconciliation for them, sayth the Lord God.
Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 All the people of the lande shall giue this oblation for the prince in Israel.
Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
17 And it shalbe ye princes part to giue burnt offrings, and meat offrings, and drinke offrings in the solemne feasts and in the newe moones, and in the Sabbaths, and in all the hie feasts of the house of Israel: he shall prepare the sinne offring, and the meat offring, and the burnt offring, and the peace offrings to make reconciliation for the house of Israel.
Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
18 Thus sayth the Lord God, In the first moneth, in the first day of the moneth, thou shalt take a yong bullocke without blemish and clense the Sanctuarie.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
19 And the Priest shall take of the blood of the sinne offring, and put it vpon the posts of the house, and vpon the foure corners of the frame of the altar, and vpon the postes of the gate of the inner court.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
20 And so shalt thou doe the seuenth day of the moneth, for euery one that hath erred and for him that is deceiued: so shall you reconcile the house.
Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
21 In the first moneth in the foureteenth day of the moneth, ye shall haue the Passeouer, a feast of seuen dayes, and ye shall eate vnleauened bread.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
22 And vpon that day, shall the prince prepare for him selfe, and for all the people of the lande, a bullocke for a sinne offring.
Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
23 And in the seuen dayes of the feast he shall make a burnt offring to the Lord, euen of seuen bullockes, and seuen rammes without blemish dayly for seuen dayes, and an hee goate dayly for a sinne offring.
Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
24 And he shall prepare a meate offring of an Ephah for a bullocke, an Ephah for a ramme, and an Hin of oyle for an Ephah.
Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
25 In the seuenth moneth, in the fifteenth day of the moneth, shall he do the like in the feast for seuen dayes, according to the sinne offring, according to the burnt offring, and according to the meate offring, and according to the oyle.
“‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”

< Ezekiel 45 >