< Ezekiel 36 >

1 Also thou sonne of man, prophesie vnto the mountaines of Israel, and say, Ye mountaines of Israel, heare the word of the Lord.
“Iwe mwana wa munthu, yankhula kwa mapiri a Israeli ndipo unene kuti, ‘Inu mapiri a Israeli, imvani mawu a Yehova.’
2 Thus saith the Lord God, because the enemie hath sayde against you, Aha, euen the hye places of the world are ours in possession,
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mdani wanu ankanena kuti, ‘Aa! Dziko lamapiri lakalekale lija lasanduka lathu.’
3 Therefore prophesie, and say, Thus sayth the Lord God, Because that they haue made you desolate, and swallowed you vp on euery side, that ye might be a possession vnto the residue of the heathen, and ye are come vnto the lippes and tongues of men, and vnto the reproch of the people,
Choncho nenera ndipo uwawuze kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anakusakazani ndi kukuponderezani ku mbali zonse motero kuti munakhala mʼmanja mwa anthu a mitundu ina yonse ndipo anthu ankakunenani ndi kukunyozani,
4 Therefore ye mountaines of Israel, heare the worde of the Lord God, Thus sayth the Lord God to the mountaines and to the hilles, to the riuers, and to the valleys, and to the waste, and desolate places, and to the cities that are forsaken: which are spoyled and had in derision of the residue of the heathen that are round about.
choncho, inu mapiri a Israeli, imvani zimene Ine Ambuye Yehova ndikuwuza mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa, mabwinja ndi mizinda yosiyidwa imene yakhala ikufunkhidwa komanso kunyozedwa ndi anthu a mitundu ina okuzungulirani.
5 Therefore thus saith the Lord God, Surely in the fire of mine indignation haue I spoken against the residue of the heathen, and against all Idumea, which haue taken my lande for their possession, with the ioy of all their heart, and with despitefull mindes to cast it out for a pray.
Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mu mkwiyo wanga woopsa ndinayankhula kuyimba mlandu mitundu ina yonse ya anthu makamaka a ku Edomu. Iwowa mwa chimwemwe chodzaza tsaya ndi mwa nkhwidzi analanda dziko langa ndi kulisandutsa lawo ndi kutengeratu dziko la msipu kukhala lawo.’
6 Prophesie therfore vpon the land of Israel, and say vnto the mountaines, and to the hilles, to the riuers, and to the valleys, Thus sayth the Lord God, Behold, I haue spoken in mine indignation, and in my wrath, because yee haue suffered the shame of the heathen,
Nʼchifukwa chake, lengeza ku dziko la Israeli, ndipo uwuze mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikuyankhula ndi mtima wokwiya kwambiri chifukwa inu munalandira chitonzo cha anthu a mitundu ina.’
7 Therefore thus saith the Lord God, I haue lifted vp mine hand, surely the heathen that are about you, shall beare their shame.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikulumbira nditakweza dzanja langa kuti mitundu ya anthu idzatozedwanso.
8 But you, O mountaines of Israel, yee shall shoote forth your branches, and bring foorth your fruite to my people of Israel: for they are ready to come.
“Koma Inu mapiri a Israeli mudzaphukanso nthambi ndipo mudzawabalira zipatso anthu anga a Israeli, pakuti ali pafupi kubwerera kwawo.
9 For behold, I come vnto you, and I wil turne vnto you, and ye shalbe tilled and sowen.
Taonani, Ine ndili mbali yanu ndipo ndidzakukomerani mtima. Mudzalimidwa ndi kudzalidwa.
10 And I wil multiply the men vpon you, euen all the house of Israel wholly, and the cities shalbe inhabited, and the desolate places shalbe builded.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha anthu anu, nyumba yonse ya Israeli. Mʼmizinda mudzakhalanso anthu ndipo mabwinja adzamangidwanso.
11 And I wil multiply vpon you man and beast, and they shall encrease, and bring fruite, and I will cause you to dwell after your olde estate, and I will bestowe benefites vpon you more then at the first, and ye shall know that I am the Lord.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha amuna pamodzi ndi ziweto zomwe, ndipo adzachuluka kwambiri ndi kubereka ana ambiri. Ndidzakhazika anthu mʼdzikomo monga analili kale, ndi kukulemeretsani kuposa kale. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
12 Yea, I wil cause men to walke vpon you, euen my people Israel, and they shall possesse you, and ye shalbe their inheritance, and ye shall no more henceforth depriue them of men.
Ndidzachititsa anthu kuyenda pa inu, ndiye kuti inu anthu anga Aisraeli. Iwowo adzakhazikika pa inu, ndipo inu mudzakhala cholowa chawo. Simudzalandanso ana awo.
13 Thus sayth the Lord God, because they say vnto you, Thou land deuourest vp men, and hast bene a waster of thy people,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anthu amanena kuti, ndiwe dziko limene limadya anthu ake ‘kulanda ana a mtundu wake,’
14 Therefore thou shalt deuoure men no more, neither waste thy people henceforth, sayth the Lord God,
nʼchifukwa chake, simudzadyanso anthu kapena kulanda ana a mtundu wako. Ine Ambuye Yehova ndikutero.
15 Neither will I cause men to heare in thee the shame of the heathen any more, neither shalt thou beare the reproche of the people any more, neither shalt cause thy folke to fal any more, saith the Lord God.
Sindidzakulolaninso kumva mnyozo wa anthu a mitundu ina, kapena kupirira kunyogodola kwawo kapenanso kupunthwitsanso anthu a mʼdziko lako. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
16 Moreouer the word of the Lord came vnto me, saying,
Yehova anandiyankhulanso kuti:
17 Sonne of man, when the house of Israel dwelt in their owne lande, they defiled it by their owne wayes, and by their deedes: their way was before me as the filthinesse of the menstruous.
“Iwe mwana wa munthu, pamene anthu a Israeli ankakhala mʼdziko lawolawo, analiyipitsa ndi makhalidwe awo ndiponso zochita zawo. Machitidwe awo pamaso panga anali onyansa pa zachipembedzo ngati msambo wa mkazi amene ali pa nthawi yake.
18 Wherfore I powred my wrath vpon them, for the blood that they had shed in the land, and for their idoles, wherewith they had polluted it.
Tsono ndinawalanga chifukwa cha magazi amene anakhetsa mʼdzikomo, ndiponso chifukwa anayipitsa dziko ndi mafano awo.
19 And I scattered them among the heathen, and they were dispersed through the countries for according to their wayes, and according to their deedes, I iudged them.
Ndinawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anabalalikira mʼmayiko onse. Ndinawalanga molingana ndi makhalidwe awo ndi zochita zawo.
20 And when they entred vnto the heathen, whither they went, they polluted mine holy Name, when they sayd of them, These are the people of the Lord, and are gone out of his land.
Atafika kwa anthu a mitundu ina, kulikonse kumene anapitako, anayipitsa dzina langa loyera. Zinatero popeza anthu ponena za iwo ankanena kuti, ‘Awa ndi anthu a Yehova, komatu anachotsedwa ku dziko lake.’
21 But I fauoured mine holy Name which the house of Israel had polluted among the heathen, whither they went.
Koma Ine ndinkadera nkhawa dzina langa loyera, limene Aisraeli analiyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapitako.
22 Therfore say vnto the house of Israel, Thus saith ye Lord God, I doe not this for your sakes, O house of Israel, but for mine holy Names sake, which yee polluted among the heathen whither ye went.
“Nʼchifukwa chake awuze Aisraeliwo kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndidzachita zimene ndidzachitezo osati chifukwa cha inuyo Aisraelinu ayi, koma chifukwa cha dzina langa, limene mwaliyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene munapitako.
23 And I wil sanctifie my great Name, which was polluted among the heathen, among whome you haue polluted it, and the heathen shall know that I am the Lord, sayth the Lord God, when I shalbe sanctified in you before their eyes.
Ndidzaonetsa chiyero cha dzina langa lotchuka, limene layipitsidwa pakati pawo. Anthu a mitundu inayo atadzazindikira kuti ndaonetsa kudzera mwa inu kuti dzina langa ndi loyera, iwo adzadziwanso kuti Ine ndine Yehova. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
24 For I will take you from among the heathen, and gather you out of all countries, and will bring you into your owne land.
“Pakuti Ine ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzakusonkhanitsani kuchoka ku mayiko onse ndi kukubwezerani ku dziko lanulanu.
25 Then wil I powre cleane water vpon you, and ye shalbe cleane: yea, from all your filthines, and from all your idoles wil I clense you.
Ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera mtima. Zonse zimene zimakuyipitsani zidzachoka. Ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.
26 A newe heart also will I giue you, and a new spirit wil I put within you, and I will take away the stonie heart out of your body, and I will giue you an heart of flesh.
Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kulowetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzachotsa mwa inu mtima wanu wowuma ngati mwala ndi kukupatsani mtima wofewa ngati mnofu.
27 And I will put my spirite within you, and cause you to walke in my statutes, and ye shall keepe my iudgements and do them.
Ndipo ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo ndidzakuthandizani kutsatira malangizo anga ndi kukusungitsani mosamala kwambiri malamulo anga.
28 And ye shall dwell in the land, that I gaue to your fathers, and ye shalbe my people, and I will be your God.
Mudzakhala mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu. Mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
29 I will also deliuer you from all your filthinesse, and I will call for corne, and will increase it, and lay no famine vpon you.
Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuyipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu ndipo sindidzakugwetseraninso njala.
30 For I will multiplie the fruite of the trees, and the increase of the fielde, that ye shall beare no more the reproch of famine among the heathen.
Ndidzachulukitsa zipatso za mʼmitengo yanu ndi zokolola za mʼmunda mwanu, kotero kuti simudzanyozedwanso pakati pa anthu a mitundu ina chifukwa cha njala.
31 Then shall ye remember your owne wicked wayes, and your deedes that were not good, and shall iudge your selues worthie to haue bene destroyed for your iniquities, and for your abominations.
Pamenepo mudzakumbukira makhalidwe anu oyipa ndi ntchito zanu zoyipa. Machimo anu ndi ntchito zanu zonyansa zidzakuchititsa nokha manyazi.
32 Be it knowen vnto you that I do not this for your sakes, sayth the Lord God: therefore, O ye house of Israel, be ashamed, and confounded for your owne wayes.
Tsono dziwani kuti Ine sindidzachita zimenezi chifukwa cha inuyo ayi, ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. Ndiyetu chitani manyazi ndipo mugwetse nkhope zanu, inu Aisraeli chifukwa cha makhalidwe anu!
33 Thus sayth the Lord God, What time as I shall haue clensed you from all your iniquities, I will cause you to dwel in the cities, and the desolate places shalbe builded.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limene ndidzayeretse machimo anu onse, ndidzayikamonso anthu mʼmizinda yanu, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja.
34 And the desolate land shalbe tilled, whereas it lay waste in the sight of all that passed by.
Dziko limene linasanduka chipululu lizidzalimidwanso. Mʼmalo moti aliyense wopitamo alione dzikolo ngati chipululu tsopano adzaliona lolimidwa.
35 For they sayd, This waste land was like the garden of Eden, and these waste and desolate and ruinous cities were strong, and were inhabited.
Iwo adzati, ‘Dziko ili, limene linali chipululu, lasanduka munda wa Edeni. Mizinda imene inali mabwinja osiyidwa ndi owonongedwa, tsopano ndi yotetezedwa ndi yokhalamo anthu.
36 Then the residue of the heathen that are left round about you, shall know that I the Lord builde the ruinous places, and plant the desolate places: I the Lord haue spoken it, and wil do it.
Ndipo anthu a mitundu ina okhala pafupi nanu amene anatsala adzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndinamanganso mizinda yowonongeka ndi kudzalanso zinthu zatsopano mʼmalo mʼmene munali chipululu. Ine Yehova ndayankhula ndipo ndidzazichitadi.’
37 Thus saith the Lord God, I will yet for this be sought of ye house of Israel, to performe it vnto them: I wil encrease them with men like a flocke.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.
38 As the holy flocke, as the flocke of Ierusalem in their solemne feastes, so shall the desolate cities be filled with flockes of men, and they shall know, that I am the Lord.
Adzachulukadi ngati nkhosa zomwe ankapereka ngati nsembe ku Yerusalemu pa nthawi za chikondwerero. Choncho mizinda ya mabwinja idzadzaza ndi anthu. Zikadzatero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 36 >