< Ezekiel 33 >

1 Again, the woorde of the Lord came vnto me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
2 Sonne of man, speake to the children of thy people, and say vnto them, When I bring the sworde vpon a lande, if the people of the lande take a man from among them, and make him their watchman,
“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
3 If when hee seeth the sworde come vpon ye land, he blow the trumpet, and warne the people,
Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
4 Then hee that heareth the sounde of the trumpet, and will not bee warned, if the sworde come, and take him away, his blood shall be vpon his owne head.
Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
5 For he heard the sound of the trumpet, and woulde not bee admonished: therefore his blood shall be vpon him: but he that receiueth warning, shall saue his life.
Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
6 But if the watchman see the sworde come, and blowe not the trumpet, and the people be not warned: if the sworde come, and take any person from among them, he is taken away for his iniquitie, but his blood will I require at the watchmans hande.
Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
7 So thou, O sonne of man, I haue made thee a watchman vnto the house of Israel: therefore thou shalt heare the woorde at my mouth, and admonish them from me.
“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
8 When I shall say vnto the wicked, O wicked man, thou shalt die the death, if thou doest not speake, and admonish the wicked of his way, that wicked man shall die for his iniquitie, but his blood will I require at thine hand.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
9 Neuerthelesse, If thou warne the wicked of his way, to turne from it, if he doe not turne from his way, he shall die for his iniquitie, but thou hast deliuered thy soule.
Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
10 Therefore, O thou sonne of man, speake vnto the house of Israel, Thus yee speake and say, If our transgressions and our sinnes bee vpon vs, and we are consumed because of them, howe should we then liue?
“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
11 Say vnto them, As I liue, sayeth the Lord God, I desire not the death of the wicked, but that the wicked turne from his way and liue: turne you, turne you from your euill waies, for why will ye die, O ye house of Israel?
Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
12 Therefore thou sonne of man, saye vnto the children of thy people, The righteousnesse of the righteous shall not deliuer him in the day of his transgression, nor the wickednesse of the wicked shall cause him to fall therein, in the day that he returneth from his wickednesse, neither shall the righteous liue for his righteousnesse in the day that he sinneth.
“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
13 When I shall say vnto the righteous, that he shall surely liue, if he trust to his owne righteousnes, and commit iniquitie, all his righteousnes shall be no more remembred, but for his iniquitie that he hath committed, he shall die for the same.
Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
14 Againe when I shall say vnto the wicked, thou shalt die the death, if he turne from his sinne, and doe that which is lawfull and right,
Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
15 To wit, if the wicked restore the pledge, and giue againe that he had robbed, and walke in the statutes of life, without committing iniquitie, he shall surely liue, and not die.
monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
16 None of his sinnes that he hath comitted, shall be mentioned vnto him: because he hath done that, which is lawful, and right, he shall surely liue.
Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
17 Yet the children of thy people say, The way of the Lord is not equall: but their owne way is vnequall.
“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
18 When the righteous turneth from his righteousnesse, and committeth iniquitie, he shall euen die thereby.
Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
19 But if the wicked returne from his wickednesse, and doe that which is lawfull and right, hee shall liue thereby.
Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
20 Yet yee say, The way of the Lord is not equall. O ye house of Israel, I will iudge you euery one after his waies.
Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
21 Also in the twelfth yere of our captiuitie, in the tenth moneth, and in the fift day of the moneth, one that had escaped out of Ierusalem, came vnto me, and said, The citie is smitten.
Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
22 Now the hand of the Lord had bene vpon me in ye euening afore hee that had escaped, came, and had opened my mouth vntill he came to me in the morning: and when hee had opened my mouth, I was no more dumme.
Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
23 Againe the worde of the Lord came vnto me, and saide,
Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
24 Sonne of man, these that dwel in the desolate places of the land of Israel, talke and say, Abraham was but one, and hee possessed the lande: but we are many, therefore the lande shall be giuen vs in possession.
“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
25 Wherefore say vnto them, Thus saieth the Lord God, Ye eate with the blood, and lift vp your eyes towarde your idoles, and sheade blood: should ye then possesse the land?
Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
26 Ye leane vpon your swordes: ye worke abomination, and yee defile euery one his neighbours wife: should ye then possesse the land?
Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
27 Say thus vnto them, Thus saieth the Lord God, As I liue, so surely they that are in the desolate places, shall fall by the sword: and him that is in the open field, will I giue vnto the beasts to be deuoured: and they that be in the forts and in the caues, shall die of the pestilence.
“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
28 For I will lay the land desolate and waste, and the pompe of her strength shall cease: and the moutaines of Israel shalbe desolate, and none shall passe through.
Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
29 Then shall they know that I am the Lord, when I haue laid ye land desolate and wast, because of al their abominations, that they haue committed.
Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
30 Also thou sonne of man, the children of thy people that talke of thee by the wals and in the dores of houses, and speake one to another, euery one to his brother, saying, Come, I pray you, and heare what is the word that commeth from the Lord.
“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
31 For they come vnto thee, as the people vseth to come: and my people sit before thee, and heare thy wordes, but they will not doe them: for with their mouthes they make iestes, and their heart goeth after their couetousnesse.
Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
32 And loe, thou art vnto them, as a iesting song of one that hath a pleasant voyce, and can sing well: for they heare thy woordes, but they doe them not.
Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
33 And when this commeth to passe (for loe, it will come) then shall they know, that a Prophet hath bene among them.
“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”

< Ezekiel 33 >