< Ezekiel 32 >
1 And in the twelfth yeere in the twelfth moneth, and in the first day of the moneth, the worde of the Lord came vnto me, saying,
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Sonne of man, take vp a lamentation for Pharaoh King of Egypt, and say vnto him, Thou art like a lyon of the nations and art as a dragon in the sea: thou castedst out thy riuers and troubledst the waters with thy feete, and stampedst in their riuers.
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
3 Thus sayth the Lord God, I will therefore spread my net ouer thee with a great multitude of people, and they shall make thee come vp into my net.
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
4 Then will I leaue thee vpon the land, and I will cast thee vpon the open field, and I wil cause all the foules of the heauen to remaine vpon thee, and I will fill all the beastes of the field with thee.
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
5 And I will lay thy flesh vpon the mountaines, and fill the valleys with thine height.
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
6 I will also water with thy blood the land wherein thou swimmest, euen to ye mountaines, and the riuers shall be full of thee.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
7 And when I shall put thee out, I will couer the heauen, and make the starres thereof darke: I will couer the sunne with a cloude, and the moone shall not giue her light.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
8 All the lightes of heauen will I make darke for thee, and bring darkenesse vpon thy lande, sayeth the Lord God.
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
9 I will also trouble the heartes of many people, when I shall bring thy destruction among the nations and vpon the countries which thou hast not knowen.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Yea, I will make many people amased at thee, and their Kings shalbe astonished with feare for thee, when I shall make my sworde to glitter against their faces, and they shall be afraide at euery moment: euery man for his owne life in the day of thy fall.
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
11 For thus sayth the Lord God, The sworde of the King of Babel shall come vpon thee.
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 By the swordes of the mightie will I cause thy multitude to fall: they all shall be terrible nations, and they shall destroy the pompe of Egypt, and all the multitude thereof shalbe consumed.
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 I will destroy also all the beastes thereof from the great watersides, neither shall the foote of man trouble them any more, nor the hooues of beast trouble them.
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Then will I make their waters deepe, and cause their riuers to runne like oyle, sayeth the Lord God.
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
15 When I shall make the land of Egypt desolate, and the countrey with all that is therein, shall be laid waste: when I shall smite all them which dwell therein, then shall they know that I am ye Lord.
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
16 This is the mourning wherewith they shall lament her: the daughters of the nations shall lament her: they shall lament for Egypt, and for all her multitude, sayeth the Lord God.
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
17 In the twelfth yeere also in the fifteenth day of the moneth, came the worde of the Lord vnto me, saying,
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
18 Sonne of man, lament for the multitude of Egypt, and cast them downe, euen them and the daughters of the mighty nations vnto the nether partes of the earth, with them that goe downe into the pit.
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
19 Whome doest thou passe in beautie? goe downe and sleepe with the vncircumcised.
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
20 They shall fall in the middes of them that are slaine by the sword: shee is deliuered to the sword: draw her downe, and all her multitude.
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
21 The most mighty and strong shall speake to him out of the mids of hell with them that helpe her: they are gone downe and sleepe with the vncircumcised that be slaine by the sworde. (Sheol )
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol )
22 Asshur is there and all his companie: their graues are about him: all they are slaine and fallen by the sworde.
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
23 Whose graues are made in the side of the pit, and his multitude are rounde about his graue: all they are slaine and fallen by the sworde, which caused feare to be in the land of the liuing.
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
24 There is Elam and all his multitude round about his graue: al they are slaine and fallen by the sword which are gone downe with the vncircumcised into the nether parts of the earth, which caused themselues to be feared in the land of the liuing, yet haue they borne their shame with them that are gone downe to the pit.
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
25 They haue made his bed in the mids of the slaine with al his multitude: their graues are round about him: all these vncircucised are slaine by the sworde: though they haue caused their feare in the land of ye liuing, yet haue they borne their shame with them that goe downe to the pitte: they are laide in the middes of them, that be slaine.
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
26 There is Meshech, Tubal, and all their multitude, their graues are round about them: al these vncircumcised were slaine by the sworde, though they caused their feare to be in ye land of the liuing.
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
27 And they shall not lie with the valiant of the vncircumcised, that are fallen, which are gone down to the graue, with their weapons of warre, and haue laied their swords vnder their heads, but their iniquitie shalbe vpon their bones: because they were the feare of the mighty in the lande of the liuing. (Sheol )
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol )
28 Yea, thou shalt be broken in the middes of the vncircumcised, and lie with them that are slaine by the sworde.
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
29 There is Edom, his Kings, and all his princes, which with their strength are laied by them that were slaine by the sworde: they shall sleepe with the vncircumcised, and with them that goe downe to the pit.
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
30 There be al the princes of the North, with al the Zidonians, which are gone downe with the slaine, with their feare: they are ashamed of their strength, and the vncircumcised sleepe with them that be slaine by the sword, and beare their shame with them that goe downe to the pit.
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
31 Pharaoh shall see them, and hee shall be comforted ouer all his multitude: Pharaoh, and all his armie shall be slaine by the sword, saieth the Lord God.
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
32 For I haue caused my feare to be in the lande of the liuing: and he shall be laid in the mids of the vncircumcised with them, that are slaine by the sword, euen Pharaoh and all his multitude, sayeth the Lord God.
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”