< Ezekiel 30 >

1 The worde of the Lord came againe vnto me, saying,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Sonne of man, prophesie, and say, Thus sayth the Lord God, Howle and cry, Wo be vnto this day.
“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
3 For the day is neere, and the day of the Lord is at hand, a cloudie day, and it shall be the time of the heathen.
Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
4 And the sword shall come vpon Egypt, and feare shall be in Ethiopia, when the slaine shall fall in Egypt, when they shall take away her multitude, and when her foundations shall be broken downe.
Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
5 Ethiopia and Phut, and Lud, and all the common people, and Cub, and the men of the land, that is in league, shall fall with them by the sword.
Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
6 Thus sayth the Lord, They also that mainteine Egypt, shall fall, and the pride of her power shall come downe: from the towre of Seueneh shall they fall by the sword, sayth the Lord God.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
7 And they shall be desolate in the middes of the countries that are desolate, and her cities shall be in the middes of the cities that are wasted.
“‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
8 And they shall knowe that I am the Lord, when I haue set a fire in Egypt, and when all her helpers shall be destroyed.
Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
9 In that day shall there messengers go forth from me in shippes, to make the carelesse Mores aftaide, and feare shall come vpon them, as in the day of Egypt: for loe, it commeth.
“‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
10 Thus sayth the Lord God, I will also make the multitude of Egypt to cease by the hand of Nebuchad-nezzar King of Babel.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
11 For he and his people with him, euen the terrible nations shall be brought to destroy the land: and they shall drawe their swordes against Egypt, and fill the land with the slaine.
Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
12 And I will make the riuers drye, and fell the land into the hands of the wicked, and I will make the land waste, and all that therein is by the hands of strangers: I the Lord haue spoken it.
Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
13 Thus saith the Lord God, I will also destroy the idoles, and I will cause their idoles to cease out of Noph, and there shall be no more a prince of the land of Egypt, and I will send a feare in the land of Egypt.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
14 And I will make Pathros desolate, and will set fire in Zoan, and I will execute iudgement in No.
Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
15 And I will powre my wrath vpon Sin, which is the strength of Egypt: and I will destroy the multitude of No.
Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
16 And I will set fire in Egypt: Sin shall haue great sorowe and No shalbe destroyed, and Noph shall haue sorowes dayly.
Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
17 The yong men of Auen, and of Phibeseth shall fall by the sworde: and these cities shall goe into captiuitie.
Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
18 At Tehaphnehes the day shall restraine his light, when I shall breake there the barres of Egypt: and when the pompe of her power shall cease in her, the cloude shall couer her, and her daughters shall goe into captiuitie.
Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
19 Thus will I execute iudgements in Egypt, and they shall knowe that I am the Lord.
Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
20 And in the eleuenth yeere, in the first moneth, and in the seuenth day of the moneth, the worde of the Lord came vnto me, saying,
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
21 Sonne of man, I haue broken the arme of Pharaoh King of Egypt: and lo, it shall not be boud vp to be healed, neither shall they put a roule to bind it, and so make it strong, to hold the sworde.
“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
22 Therefore thus saith the Lord God, Behold, I come against Pharaoh King of Egypt, and will breake his arme, that was strong, but is broken, and I will cause the sworde to fall out of his hande.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
23 And I will scatter the Egyptians among the nations, and will disperse them through the countreys.
Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
24 And I will strengthen the arme of the King of Babel, and put my sworde in his hand, but I will breake Pharaohs armes, and he shall cast out sighings, as the sighings of him, that is wounded before him.
Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
25 But I will strengthen the armes of the king of Babel, and the armes of Pharaoh shall fall downe, and they shall knowe, that I am the Lord, when I shall put my sworde into the hand of the King of Babel, and he shall stretch it out vpon the land of Egypt.
Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
26 And I will scatter the Egyptians among the nations, and disperse them among ye countreys, and they shall knowe, that I am the Lord.
Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 30 >