< Ezekiel 29 >
1 In the tenth yeere, and in the tenth moneth in the twelfth day of the moneth, the word of the Lord came vnto me, saying,
Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Sonne of man, set thy face against Pharaoh the King of Egypt, and prophecie against him, and against all Egypt.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
3 Speake, and say, Thus sayth the Lord God, Beholde, I come against thee, Pharaoh King of Egypt, the great dragon, that lieth in the middes of his riuers, which hath saide, The riuer is mine, and I haue made it for my selfe.
Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
4 But I will put hookes in thy chawes, and I will cause the fish of thy riuers to sticke vnto thy scales, and I will drawe thee out of the middes of thy riuers, and all the fishe of thy riuers shall sticke vnto thy scales.
Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
5 And I will leaue thee in the wildernes, both thee and al the fish of thy riuers: thou shalt fal vpon ye open field: thou shalt not be brought together, nor gathered: for I haue giue thee for meat to the beasts of the field, and to the foules of heauen.
Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
6 And al the inhabitants of Egypt shall know that I am the Lord, because they haue ben a staffe of reede to the house of Israel.
Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
7 When they tooke holde of thee with their hand, thou diddest breake, and rent all their shoulder: and when they leaned vpon thee, thou brakest and madest all their loynes to stand vpright.
Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
8 Therefore thus sayeth the Lord God, Beholde, I will bring a sworde vpon thee, and destroy man and beast out of thee,
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
9 And the land of Egypt shalbe desolate, and waste, and they shall know that I am ye Lord: because he hath said, The riuer is mine, and I haue made it,
Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
10 Behold, therefore I come vpon thee, and vpon thy riuers, and I will make the land of Egypt vtterly waste and desolate from the towre of Seueneh, euen vnto the borders of the blacke Mores.
nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
11 No foote of man shall passe by it, nor foote of beast shall passe by it, neither shall it be inhabited fourtie yeeres.
Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
12 And I wil make the land of Egypt desolate in the middes of the countries, that are desolate, and her cities shall be desolate among the cities that are desolate, for fourtie yeeres: and I wil scatter the Egyptians among the nations, and wil disperse them through the countreis.
Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
13 Yet thus saieth the Lord God, At the end of fourtie yeeres will I gather the Egyptians from the people, where they were scattered,
“‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
14 And I wil bring againe the captiuitie of Egypt, and will cause them to returne into the land of Pathros, into the lande of their habitation, and they shalbe there a small kingdome.
Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
15 It shall be the smallest of the kingdomes, neither shall it exalt it selfe any more aboue the nations: for I will diminish them, that they shall no more rule the nations.
Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
16 And it shall be no more the confidence of the house of Israel, to bring their iniquitie to remembrance by looking after them, so shall they knowe, that I am the Lord God.
Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
17 In the seuen and twentieth yeere also in the first moneth, and in the first day of the moneth, came the word of the Lord vnto me, saying,
Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
18 Sonne of man, Nebuchad-nezzar King of Babel caused his armie to serue a great seruice against Tyrus: euery head was made balde, and euery shoulder was made bare: yet had he no wages, nor his armie for Tyrus, for the seruice that he serued against it.
“Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
19 Therefore thus sayth the Lord God, Beholde, I will giue the land of Egypt vnto Nebuchad-nezzar the King of Babel, and he shall take her multitude, and spoyle her spoyle, and take her pray, and it shall be the wages for his armie.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
20 I haue giuen him the land of Egypt for his labour, that he serued against it, because they wrought for me, sayth the Lord God.
Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
21 In that day will I cause the horne of the house of Israel to growe, and I will giue thee an open mouth in the middes of them, and they shall knowe that I am the Lord.
“Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”