< Ezekiel 27 >

1 The worde of the Lord came againe vnto me, saying,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Sonne of man, take vp a lametation for Tyrus,
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 And say vnto Tyrus, that is situate at the entrie of the sea, which is the marte of the people for many yles, Thus sayeth the Lord God, O Tyrus, thou hast said, I am of perfite beautie.
Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 Thy borders are in the middes of the sea, and thy builders haue made thee of perfit beauty.
Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 They haue made all thy shippe boardes of firre trees of Shenir: they haue brought cedars from Lebanon, to make mastes for thee.
Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
6 Of ye okes of Bashan haue they made thine ores: the company of the Assyrians haue made thy banks of yuorie, brought out of ye yles of Chittim.
Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Fine linen with broydered woorke, brought from Egypt, was spread ouer thee to be thy sayle, blue silke and purple, brought from the yles of Elishah, was thy couering.
Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
8 The inhabitants of Zidon, and Aruad were thy mariners, O Tyrus: thy wise men that were in thee, they were thy pilots.
Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 The ancients of Gebal, and the wise men thereof were in thee thy calkers, all the shippes of the sea with their mariners were in thee to occupie thy marchandise.
Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 They of Persia, and of Lud and of Phut were in thine armie: thy men of warre they hanged the shielde and helmet in thee: they set foorth thy beautie.
“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 The men of Aruad with thine armie were vpon thy walles round about, and the Gammadims were in thy towres: they hanged their shields vpon thy walles round about: they haue made thy beautie perfite.
Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 They of Tarshish were thy marchantes for the multitude of all riches, for siluer, yron, tynne, and leade, which they brought to thy faires.
“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 They of Iauan, Tubal and Meshech were thy marchants, concerning the liues of men, and they brought vessels of brasse for thy marchadise.
“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 They of the house of Togarmah brought to thy faires horses, and horsemen, and mules.
“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 The men of Dedan were thy marchantes: and the marchandise of many yles were in thine handes: they brought thee for a present hornes, teeth, and peacockes.
“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 They of Aram were thy marchants for the multitude of thy wares: they occupied in thy faires with emerauds, purple, and broidred worke, and fine linen, and corall, and pearle.
“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 They of Iudah and of the land of Israel were thy marchants: they brought for thy marchandise wheat of Minnith, and Pannag, and honie and oyle, and balme.
“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 They of Damascus were thy marchants in ye multitude of thy wares, for the multitude of all riches, as in the wine of Helbon and white wooll.
“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
19 They of Dan also and of Iauan, going to and from, occupied in thy faires: yron woorke, cassia and calamus were among thy marchandise.
Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 They of Dedan were thy marchants in precious clothes for the charets.
“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 They of Arabia, and all the princes of Kedar occupied with thee, in lambes, and rammes and goates: in these were they thy marchants.
“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 The marchats of Sheba, and Raamah were thy marchantes: they occupied in thy faires with the chiefe of all spices, and with al precious stones and golde.
“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 They of Haram and Canneh and Eden, the marchants of Sheba, Asshur and Chilmad were thy marchants.
“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 These were thy marchants in all sortes of things, in raiment of blewe silke, and of broydred woorke, and in coffers for the rich apparell, which were bound with cordes: chaines also were among thy marchandise.
Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 The shippes of Tarshish were thy chiefe in thy marchandise, and thou wast replenished and made very glorious in the middes of the sea.
“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Thy robbers haue brought thee into great waters: the East winde hath broken thee in the middes of the sea.
Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
27 Thy riches and thy faires, thy marchandise, thy mariners and pilotes, thy calkers, and the occupiers of thy marchandise and al thy men of warre that are in thee, and all thy multitude which is in the middes of thee, shall fall in the middes of the sea in the day of thy ruine.
Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
28 The suburbes shall shake at the sound of the crie of thy pilotes.
Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 And all that handle the ore, the mariners and al the pilots of the sea shall come downe from their shippes, and shall stand vpon the land,
Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 And shall cause their voyce to be heard against thee, and shall cry bitterly, and shall cast dust vpon their heads, and wallow theselues in the ashes.
Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 They shall plucke off their heare for thee and gird them with a sackecloth, and they shall weepe for thee with sorow of heart and bitter mourning.
Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
32 And in their mourning, they shall take vp a lametation for thee, saying, What citie is like Tyrus, so destroied in the middes of the sea!
Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
33 When thy wares went foorth of the seas, thou filledst many people, and thou diddest enrich the Kings of the earth with the multitude of thy riches and of thy marchandise.
Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
34 When thou shalt be broken by ye seas in the depths of the waters, thy marchandise and all thy multitude, which was in the mids of thee, shall fal.
Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
35 All the inhabitantes of the yles shall be astonished at thee, and all their Kings shall be sore afraide and troubled in their countenance.
Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
36 The marchants among the people shall hisse at thee: thou shalt be a terrour, and neuer shalt be any more.
Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

< Ezekiel 27 >