< Exodus 9 >
1 Then the Lord said vnto Moses, Go to Pharaoh, and tell him, Thus saith the Lord God of the Ebrewes, Let my people go, that they may serue me.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
2 But if thou refuse to let them goe, and wilt yet holde them still,
Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
3 Beholde, the hande of the Lord is vpon thy flocke which is in the fielde: for vpon the horses, vpon the asses, vpon the camels, vpon the cattell, and vpon the sheepe shalbe a mightie great moraine.
dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
4 And the Lord shall doe wonderfully betweene the beastes of Israel, and the beastes of Egypt: so that there shall nothing dye of all, that pertaineth to the children of Israel.
Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
5 And the Lord appointed a time, saying, To morowe the Lord shall finish this thing in this lande.
Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
6 So the Lord did this thing on the morow, and all the cattel of Egypt dyed: but of the cattell of the children of Israel dyed not one.
Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
7 Then Pharaoh sent, and beholde, there was not one of the cattell of the Israelites dead: and the heart of Pharaoh was obstinate, and hee did not let the people goe.
Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
8 And the Lord said to Moses and to Aaron, Take your handfull of ashes of the fornace, and Moses shall sprinkle them towarde the heauen in the sight of Pharaoh,
Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
9 And they shall be turned to dust in all the land of Egypt: and it shalbe as a scab breaking out into blisters vpon man, and vpon beast, thorow out all the land of Egypt.
Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
10 Then they tooke ashes of the fornace, and stoode before Pharaoh: and Moses sprinkled them towarde the heauen, and there came a scab breaking out into blisters vpon man, and vpon beast.
Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
11 And the sorcerers could not stande before Moses, because of the scab: for the scab was vpon the enchanters, and vpon all the Egyptians.
Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
12 And the Lord hardened the heart of Pharaoh, and he hearkened not vnto them, as the Lord had said vnto Moses.
Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
13 Also the Lord said vnto Moses, Rise vp early in the morning, and stand before Pharaoh, and tell him, Thus saith the Lord God of the Ebrewes, Let my people goe, that they may serue me.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
14 For I will at this time send all my plagues vpon thine heart, and vpon thy seruants, and vpon thy people, that thou mayest knowe that there is none like me in all the earth.
Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
15 For nowe I will stretch out mine hande, that I may smite thee and thy people with the pestilence: and thou shalt perish from the earth.
Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
16 And in deede, for this cause haue I appointed thee, to shewe my power in thee, and to declare my Name throughout all the world.
Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
17 Yet thou exaltest thy selfe against my people, and lettest them not goe.
Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
18 Beholde, to morowe this time I will cause to raine a mightie great haile, such as was not in Egypt since the foundation thereof was laid vnto this time.
Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
19 Send therefore nowe, and gather the cattell, and all that thou hast in the fielde: for vpon all the men, and the beastes, which are found in the field, and not brought home, the haile shall fall vpon them, and they shall die.
Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
20 Such then as feared the word of the Lord among the seruants of Pharaoh, made his seruants and his cattell flee into the houses:
Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
21 But such as regarded not the worde of the Lord, left his seruants, and his cattell in the fielde.
Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
22 And the Lord saide to Moses, Stretche foorth thine hande towarde heauen, that there may be haile in all the land of Egypt, vpon man, and vpon beast, and vpon all the herbes of the fielde in the lande of Egypt.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
23 Then Moses stretched out his rod towarde heauen, and the Lord sent thunder and haile, and lightening vpon the ground: and the Lord caused haile to raine vpon the land of Egypt.
Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
24 So there was haile, and fire mingled with the haile, so grieuous, as there was none throughout all the lande of Egypt, since it was a nation.
Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
25 And the haile smote throughout al ye land of Egypt all that was in the fielde, both man and beast: also ye haile smote all the herbes of ye field, and brake to pieces all the trees of the fielde.
Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
26 Onely in the lande of Goshen (where the children of Israel were) was no haile.
Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
27 Then Pharaoh sent and called for Moses and Aaron, and said vnto them, I haue now sinned: the Lord is righteous, but I and my people are wicked.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
28 Pray ye vnto the Lord (for it is ynough) that there be no more mightie thunders and haile, and I will let you goe, and yee shall tarie no longer.
Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
29 Then Moses saide vnto him, Assoone as I am out of the citie, I will spreade mine hands vnto the Lord, and the thunder shall cease, neither shall there be any more haile, that thou mayest knowe that the earth is the Lordes.
Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
30 As for thee and thy seruants, I knowe afore I pray ye will feare before the face of the Lord God.
Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
31 (And the flaxe, and the barley were smitten: for the barley was eared, and the flaxe was bolled.
Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
32 But the wheat and the rye were not smitten, for they were hid in the grounde)
Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
33 Then Moses went out of the citie from Pharaoh, and spred his hands to the Lord, and the thunder and the haile ceased, neither rained it vpon the earth.
Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
34 And when Pharaoh sawe that the raine and the haile and the thunder were ceased, hee sinned againe, and hardened his heart, both he, and his seruants.
Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
35 So the heart of Pharaoh was hardened: neither would he let the children of Israel goe, as the Lord had said by Moses.
Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.