< Exodus 8 >

1 Afterward the Lord sayde vnto Moses, Goe vnto Pharaoh, and tell him, Thus saith the Lord, Let my people goe, that they may serue me:
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 And if thou wilt not let them goe, beholde, I will smite all thy countrey with frogges:
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 And the riuer shall scral ful of frogges, which shall goe vp and come into thine house, and into thy chamber, where thou sleepest, and vpon thy bed, and into the house of thy seruants, and vpon thy people, and into thine ouens, and into thy kneading troughes.
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 Yea, the frogges shall climbe vp vpon thee, and on thy people, and vpon all thy seruants.
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 Also the Lord said vnto Moses, Say thou vnto Aaron, Stretch out thine hande with thy rod vpon the streames, vpon the riuers, and vpon the ponds, and cause frogs to come vp vpon the land of Egypt.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 Then Aaron stretched out his hand vpon the waters of Egypt, and the frogges came vp, and couered the land of Egypt.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 And the sorcerers did likewise with their sorceries, and brought frogges vp vpon the land of Egypt.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Then Pharaoh called for Moses and Aaron, and said, Pray ye vnto the Lord, that hee may take away the frogges from mee, and from my people, and I will let the people goe, that they may doe sacrifice vnto the Lord.
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 And Moses said vnto Pharaoh, Concerning me, euen command when I shall pray for thee, and for thy seruants, and for thy people, to destroy the frogges from thee and from thine houses, that they may remaine in the riuer only.
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 Then he said, To morowe. And he answered, Be it as thou hast said, that thou maiest know, that there is none like vnto the Lord our God.
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 So the frogges shall depart from thee, and from thine houses, and from thy seruantes, and from thy people: onely they shall remaine in the riuer.
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Then Moses and Aaron went out from Pharaoh: and Moses cryed vnto the Lord concerning the frogges, which hee had sent vnto Pharaoh.
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 And the Lord did according to the saying of Moses: so the frogges died in the houses, in the townes, and in the fieldes.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 And they gathered the together by heaps, and the land stanke of them.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 But when Pharaoh sawe that hee had rest giuen him, he hardened his heart, and hearkened not vnto them, as the Lord had said.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 Againe the Lord sayd vnto Moses, Say vnto Aaron, Stretche out the rod, and smite the dust of the earth, that it may bee turned to lyce throughout all the land of Egypt.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 And they did so: for Aaron stretched out his hand with his rod, and smote the dust of the earth: and lyce came vpon man and vpon beast: all the dust of the earth was lyce throughout all the land of Egypt.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 Nowe the enchanters assaied likewise with their enchantments to bring forth lyce, but they could not. So the lyce were vpon man and vpon beast.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 Then saide the enchanters vnto Pharaoh, This is the finger of God. But Pharaohs heart remained obstinate, and hee hearkened not vnto them, as the Lord had said.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 Moreouer the Lord sayd to Moses, Rise vp earely in the morning, and stand before Pharaoh (lo, hee will come forth vnto the water) and say vnto him, Thus saith the Lord, Let my people go, that they may serue me.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 Els, if thou wilt not let my people goe, behold, I will send swarmes of flies both vpon thee, and vpon thy seruants, and vpon thy people, and into thine houses: and the houses of the Egyptians shalbe full of swarmes of flies, and the ground also whereon they are.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 But ye land of Goshe, where my people are, wil I cause to be wonderfull in that day, so that no swarmes of flies shalbe there, that thou maiest know that I am the Lord in the middes of the earth.
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 And I will make a deliuerance of my people from thy people: to morowe shall this miracle be.
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 And the Lord did so: for there came great swarmes of flies into the house of Pharaoh, and into his seruants houses, so that through all the lande of Egypt, the earth was corrupt by the swarmes of flies.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Then Pharaoh called for Moses and Aaron, and saide, Goe, doe sacrifice vnto your God in this lande.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 But Moses answered, It is not meete to do so: for then we shoulde offer vnto the Lord our God that, which is an abomination vnto the Egyptians. Loe, can we sacrifice the abomination of the Egyptians before their eyes, and they not stone vs?
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 Let vs go three dayes iourney in the desert, and sacrifice vnto the Lord our God, as he hath commanded vs.
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 And Pharaoh said, I will let you go, that ye may sacrifice vnto the Lord your God in the wildernesse: but goe not farre away, pray for me.
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 And Moses said, Behold, I will go out from thee, and pray vnto the Lord, that the swarmes of flies may depart from Pharaoh, from his seruants, and from his people to morowe: but let Pharaoh from hencefoorth deceiue no more, in not suffering the people to sacrifice vnto the Lord.
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 So Moses went out from Pharaoh and prayed vnto the Lord.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 And the Lord did according to the saying of Moses, and the swarmes of flies departed from Pharaoh, from his seruants, and from his people, and there remained not one.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 Yet Pharaoh hardened his heart at this time also, and did not let the people goe.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

< Exodus 8 >