< Exodus 36 >

1 Then wrought Bezaleel, and Aholiab, and all cunning men, to whome the Lord gaue wisedome, and vnderstanding, to knowe howe to worke all maner worke for the seruice of the Sanctuarie, according to all that the Lord had commanded.
Choncho Bezaleli, Oholiabu pamodzi ndi anthu aluso onse amene Yehova anawapatsa luso ndi nzeru zodziwira kupanga zofunika zonse zomangira malo opatulika, adzapanga zonse iwowo, monga momwe Yehova analamulira.”
2 For Moses had called Bezaleel, and Aholiab, and all the wise hearted men, in whose heartes the Lord had giuen wisedome, euen as many as their hearts encouraged to come vnto that worke to worke it.
Ndipo Mose anayitana Bezaleli ndi Oholiabu ndiponso munthu aliyense waluso amene Yehova anamupatsa luso ndiponso amene anali ndi mtima wofuna kugwira ntchito.
3 And they receiued of Moses all the offering which the children of Israel had brought for the worke of the seruice of the Sanctuary, to make it: also they brought still vnto him free giftes euery morning.
Iwo analandira kuchokera kwa Mose zopereka zonse Aisraeli anabweretsa kuti agwirire ntchito yomanga malo wopatulika. Ndipo anthu anapitirira kupereka zopereka zaufulu mmawa uliwonse.
4 So all the wise men, that wrought all the holy worke, came euery man from his worke which they wrought,
Kotero amisiri onse amene amagwira ntchito yonse ya malo wopatulika anasiya ntchitoyo
5 And spake to Moses, saying, The people bring too much, and more then ynough for the vse of the worke, which the Lord hath commanded to be made.
ndipo anati kwa Mose, “Anthu akubweretsa kuposa zimene zikufunika kugwirira ntchito imene Yehova analamulira kuti ichitike.”
6 Then Moses gaue a commandement, and they caused it to be proclaymed throughout the hoste, saying, Let neither man nor woman prepare any more worke for the oblation of the Sanctuarie. So the people were stayed from offring.
Choncho Mose analamulira ndipo analengeza mu msasa onse, “Mwamuna kapena mayi aliyense asaperekenso chopereka chilichonse cha ku malo wopatulika.” Choncho anthu analetsedwa kubweretsa zambiri,
7 For the stuffe they had, was sufficient for all the worke to make it, and too much.
chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.
8 All the cunning men therefore among the workemen, made for the Tabernacle ten curtaines of fine twined linnen, and of blewe silke, and purple, and skarlet: Cherubims of broydred worke made they vpon them.
Anthu onse aluso pakati pa anthu ogwira ntchitoyo anapanga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso anapeta pa nsaluzo Akerubi.
9 The length of one curtaine was twentie and eight cubits, and the breadth of one curtaine foure cubites: and the curtaines were all of one cise.
Nsalu zonse zinali zofanana. Mulitali mwake zinali mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
10 And he coupled fiue curtaines together, and other fiue coupled he together.
Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
11 And he made strings of blewe silke by the edge of one curtaine, in the seluedge of the coupling: likewise he made on the side of the other curtaine in the seluedge in the second coupling.
Kenaka anapanga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
12 Fiftie strings made he in the one curtaine, and fiftie strings made he in the edge of the other curtaine, which was in the second coupling: the strings were set one against another.
Iwo anasokerera zokolowekamo makumi asanu pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Anapanga kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
13 After, he made fiftie taches of golde, and coupled the curtaines one to another with the taches: so was it one Tabernacle.
Kenaka anapanga ngowe zagolide 50 zolumikizira nsalu ziwirizo kotero kuti zinapanga chihema chimodzi.
14 Also he made curtaines of goates heare for the couering vpon the Tabernacle: he made them to the nomber of eleuen curtaines.
Iwo anapanga nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zinalipo khumi ndi imodzi.
15 The length of one curtaine had thirtie cubites, and the bredth of one curtaine foure cubites: the eleuen curtaines were of one cise.
Nsalu zonse khumi ndi imodzi zinali zofanana. Mulitali mwake munali mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake munali mamita awiri.
16 And hee coupled fiue curtaines by themselues, and sixe curtaines by themselues:
Iwo analumikiza nsalu zisanu kukhala nsalu imodzi ndipo nsalu zinazo zisanu ndi imodzi, analumikizanso kukhala nsalu imodzinso.
17 Also he made fiftie strings vpon the edge of one curtaine in the seluedge in the coupling, and fiftie strings made hee vpon the edge of the other curtaine in the second coupling.
Kenaka anasokerera zokolowekamo makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija ndiponso anapanga zokolowekamo zina makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
18 He made also fiftie taches of brasse to couple the couering that it might be one.
Iwo anapanga ngowe 50 zamkuwa zolowetsa mu zokolowekazo ndipo anaphatikiza nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
19 And he made a couering vpon the pauilion of rams skinnes dyed red, and a couering of badgers skinnes aboue.
Ndipo anapanga chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake anapanganso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
20 Likewise he made the boards for the Tabernacle, of Shittim wood to stand vp.
Iwo anapanga maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
21 The length of a board was ten cubites, and the bredth of one board was a cubite, and an halfe.
Feremu iliyonse inali yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake munali masentimita 69.
22 One board had two tenons, set in order as the feete of a ladder, one against another: thus made he for all the boardes of the Tabernacle.
Thabwa lililonse linali ndi zolumikizira ziwiri. Iwo anapanga maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
23 So he made twentie boardes for the South side of the Tabernacle, euen full South.
Anapanga maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho,
24 And fourtie sockets of siluer made he vnder the twentie boardes, two sockets vnder one board for his two tenons, and two sockets vnder another board for his two tenons.
ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
25 Also for the other side of the Tabernacle toward the North, he made twentie boards,
Iwo anapanganso maferemu makumi awiri a mbali yakumpoto ya chihemacho,
26 And their fourtie sockets of siluer, two sockets vnder one board, and two sockets vnder another boarde.
ndiponso matsinde makumi anayi asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
27 Likewise toward the Westside of the Tabernacle he made sixe boardes.
Anapanganso maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo,
28 And two boardes made he in the corners of the Tabernacle, for either side,
ndiponso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
29 And they were ioyned beneath, and likewise were made sure aboue with a ring: thus he did to both in both corners.
Pa ngodya ziwirizi panali maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba atalumikizidwa pa ngowe imodzi. Maferemu onse anali ofanana.
30 So there were eight boards and their sixteene sockets of siluer, vnder euery board two sockets.
Choncho panali maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri anali pansi pa feremu iliyonse.
31 After, he made barres of Shittim wood, fiue for the boards in ye one side of ye Tabernacle,
Iwo anapanganso mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha. Mitanda isanu inali ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
32 And fiue barres for the boardes in the other side of the Tabernacle, and fiue barres for the boards of the Tabernacle on the side toward the West.
mitanda isanu inanso inali ya maferemu a mbali inayo ndipo mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
33 And he made the middest barre to shoote through the boards, from the one end to ye other.
Anapanga mtanda wapakati omwe umachokera pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
34 He ouerlayd also the boards with gold, and made their rings of gold for places for the barres, and couered the barres with golde.
Iwo anakuta maferemuwo ndi golide ndiponso anapanga mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso anayikuta ndi golide.
35 Moreouer he made a vaile of blew silke, and purple, and of skarlet, and of fine twined linen: with Cherubims of broydred worke made he it:
Anapanga nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo inali yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso anapetapo zithunzi za Akerubi.
36 And made thereunto foure pillars of Shittim, and ouerlayd them with golde: whose hookes were also of golde, and hee cast for them foure sockets of siluer.
Iwo anapanga nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide. Anapanganso ngowe zagolide za nsanamirazo ndi matsinde asiliva anayi.
37 And he made an hanging for the Tabernacle doore, of blew silke, and purple, and skarlet, and fine twined linnen, and needle worke,
Anapanga nsalu ya pa chipata cholowera mu chihema, yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira yomwe inali yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
38 And the fiue pillars of it with their hookes, and ouerlayde their chapiters and their filets with golde, but their fiue sockets were of brasse.
Anapanga nsanamira zisanu ndi ngowe zake. Anakuta pamwamba pa nsanamirazo ndi zomangira zake ndi golide, ndipo anapanganso matsinde asanu amkuwa.

< Exodus 36 >