< Exodus 27 >
1 Moreouer thou shalt make the altar of Shittim wood, fiue cubites long and fiue cubites broade (the altar shall be foure square) and the height thereof three cubites.
“Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
2 And thou shalt make it hornes in the foure corners thereof: the hornes shalbe of it selfe, and thou shalt couer it with brasse.
Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
3 Also thou shalt make his ashpannes for his ashes and his besoms, and his basens, and his flesh-hookes, and his censers: thou shalt make all the instruments thereof of brasse.
Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 And thou shalt make vnto it a grate like networke of brasse: also vpon that grate shalt thou make foure brasen rings vpon the foure corners thereof.
Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
5 And thou shalt put it vnder the compasse of the altar beneath, that the grate may be in the middes of the altar.
Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
6 Also thou shalt make barres for the altar, barres, I say, of Shittim wood, and shalt couer them with brasse.
Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
7 And the barres thereof shalbe put in the rings, the which barres shalbe vpon the two sides of the altar to beare it.
Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
8 Thou shalt make the altar holowe betweene the boardes: as God shewed thee in the mount, so shall they make it.
Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
9 Also thou shalt make the court of the Tabernacle in the Southside, euen full South: the court shall haue curtaines of fine twined linnen, of an hundreth cubites long, for one side,
“Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 And it shall haue twentie pillars, with their twentie sockets of brasse: the heades of the pillars, and their filets shalbe siluer.
Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 Likewise on the Northside in length there shalbe hangings of an hundreth cubites long, and the twentie pillars thereof with their twentie sockets of brasse: the heades of the pillars and the filets shalbe siluer.
Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 And the breadth of the court on the Westside shall haue curtaines of fiftie cubites, with their ten pillars and their ten sockets.
“Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
13 And the breadth of the court, Eastwarde full East shall haue fiftie cubites.
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
14 Also hangings of fifteene cubites shalbe on the one side with their three pillars and their three sockets.
Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
15 Likewise on the other side shalbe hangings of fifteene cubites, with their three pillars and their three sockets.
Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 And in the gate of the court shalbe a vaile of twentie cubites, of blewe silke, and purple, and skarlet, and fine twined linen wrought with needle, with the foure pillars thereof and their foure sockets.
“Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
17 All the pillars of the court shall haue filets of siluer round about, with their heads of siluer, and their sockets of brasse.
Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
18 The length of the court shalbe an hundreth cubites, and the breadth fiftie at either ende, and the height fiue cubites, and the hangings of fine twined linen, and their sockets of brasse.
Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
19 Al the vessels of the Tabernacle for al maner seruice thereof, and all the pinnes thereof, and all the pinnes of the court shalbe brasse.
Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
20 And thou shalt commande the children of Israel, that they bring vnto thee pure oyle oliue beaten, for the light, that the lampes may alway burne.
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
21 In the Tabernacle of the Congregation without the vaile, which is before the Testimony, shall Aaron and his sonnes dresse them from euening to morning before the Lord, for a statute for euer vnto their generations, to be obserued by the children of Israel.
Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”