< Exodus 13 >

1 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anati kwa Mose,
2 Sanctifie vnto me all the first borne: that is, euery one that first openeth the wombe among the children of Israel, as well of man as of beast: for it is mine.
“Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
3 Then Moses sayd vnto the people, Remember this day in the which ye came out of Egypt, out of the house of bondage: for by a mightie hande the Lord brought you out from thence: therefore no leauened bread shall bee eaten.
Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
4 This day come yee out in the moneth of Abib.
Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
5 Now when the Lord hath brought thee into the land of the Canaanites, and Hittites, and Amorites, and Hiuites, and Iebusites (which he sware vnto thy fathers, that he woulde giue thee, a land flowing with milke and honie) then thou shalt keepe this seruice in this moneth.
Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
6 Seuen dayes shalt thou eate vnleauened bread, and the seuenth day shall be the feast of the Lord.
Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
7 Vnleauened bread shall bee eaten seuen dayes, and there shall no leauened bread be seene with thee, nor yet leauen be seene with thee in all thy quarters.
Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
8 And thou shalt shew thy sonne in that day, saying, This is done, because of that which the Lord did vnto me, when I came out of Egypt.
Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
9 And it shalbe a signe vnto thee vpon thine hande, and for a remembrance betweene thine eyes, that the Lawe of the Lord may be in thy mouth: for by a strong hand the Lord brought thee out of Egypt.
Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
10 Keepe therefore this ordinance in his season appoynted from yeere to yeere.
Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
11 And when the Lord shall bring thee into the lande of the Canaanites, as hee sware vnto thee and to thy fathers, and shall giue it thee,
“Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
12 Then thou shalt set apart vnto the Lord all that first openeth the wombe: also euery thing that first doeth open the wombe, and commeth forth of thy beast: the males shalbe the Lordes.
muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
13 But euery first foale of an asse, thou shalt redeeme with a lambe: and if thou redeeme him not, then thou shalt breake his necke: likewise all the first borne of man among thy sonnes shalt thou bye out.
Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
14 And when thy sonne shall aske thee to morowe, saying, What is this? thou shalt then say vnto him, With a mightie hande the Lord brought vs out of Egypt, out of the house of bondage.
“Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
15 For when Pharaoh was harde hearted against our departing, the Lord then slewe all the first borne in the lande of Egypt: from the first borne of man euen to the first borne of beast: therefore I sacrifice vnto the Lord all the males that first open the wombe, but all the first borne of my sonnes I redeeme.
Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
16 And it shalbe as a token vpon thine hand, and as frontlets betweene thine eyes, that the Lord brought vs out of Egypt by a mightie hande.
Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
17 Nowe when Pharaoh had let the people go, God caried them not by the way of the Philistims countrey, though it were neerer: (for God sayd, Lest the people repent whe they see warre, and turne againe to Egypt)
Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
18 But God made the people to go about by the way of the wildernesse of the red sea: and the children of Israel went vp armed out of the land of Egypt.
Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
19 (And Moses tooke the bones of Ioseph with him: for he had made the children of Israel sweare, saying, God will surely visite you, and ye shall take my bones away hence with you)
Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
20 So they tooke their iourney from Succoth, and camped in Etham in the edge of the wildernesse.
Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
21 And the Lord went before them by day in a pillar of a cloude to leade them the way, and by night in a pillar of fire to giue them light, that they might go both by day and by night.
Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
22 He tooke not away the pillar of ye cloude by day, nor the pillar of fire by night from before the people.
Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.

< Exodus 13 >