< Esther 6 >

1 The same night the King slept not, and he comanded to bring ye booke of the records, and the chronicles: and they were read before ye King.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 Then it was found written that Mordecai had tolde of Bigtana, and Teresh two of the Kings eunuches, keepers of the dore, who sought to lay hands on the King Ahashuerosh.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 Then the King sayde, What honour and dignitie hath bene giuen to Mordecai for this? And the Kings seruants that ministred vnto him, sayd, There is nothing done for him.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 And the King sayde, Who is in the court? (Now Haman was come into the inner court of the Kings house, that he might speake vnto the King to hang Mordecai on the tree that he had prepared for him.)
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 And the Kings seruants said vnto him, Behold, Haman standeth in the court. And the King sayd, Let him come in.
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 And when Haman came in, the King saide vnto him, What shalbe done vnto ye man, whom the King will honour? Then Haman thought in his heart, To whom would the King do honour more then to me?
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 And Haman answered the King, The man whome the King would honour,
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 Let them bring for him royall apparell, which the King vseth to weare, and the horse that the King rideth vpon, and that the crowne royall may be set vpon his head.
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 And let the raiment and the horse be deliuered by the hand of one of the Kings most noble princes, and let them apparel the man (whome the King will honour) and cause him to ride vpon the horse thorow the streete of the citie, and proclayme before him, Thus shall it be done vnto the man, whome the King will honour.
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 Then the King said to Haman, Make haste, take the rayment and the horse as thou hast said, and doe so vnto Mordecai the Iewe, that sitteth at the Kings gate: let nothing fayle of all that thou hast spoken.
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 So Haman tooke the rayment and the horse, and arayed Mordecai, and brought him on horse backe thorowe the streete of the citie, and proclaymed before him, Thus shall it be done to the man whom the King will honour.
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 And Mordecai came againe to the Kings gate, but Haman hasted home mourning and his head couered.
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 And Haman tolde Zeresh his wife, and all his friends all that had befallen him. Then sayd his wise men, and Zeresh his wife vnto him, If Mordecai be of the seede of the Iewes, before whom thou hast begunne to fall; thou shalt not preuaile against him, but shalt surely fall before him.
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 And while they were yet talking with him, came the Kings eunuches and hasted to bring Haman vnto the banket that Ester had prepared.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.

< Esther 6 >