< Deuteronomy 8 >

1 Ye shall keepe all the commandements which I command thee this day, for to doe them: that ye may liue, and be multiplied, and goe in, and possesse the land which the Lord sware vnto your fathers.
Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
2 And thou shalt remember all ye way which the Lord thy God led thee this fourtie yeere in the wildernesse, for to humble thee and to proue thee, to knowe what was in thine heart, whether thou wouldest keepe his commandements or no.
Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
3 Therefore he humbled thee, and made thee hungry, and fed thee with MAN, which thou knewest not, neither did thy fathers know it, that he might teache thee that man liueth not by bread onely, but by euery worde that proceedeth out of the mouth of the Lord, doth a man liue.
Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
4 Thy raiment waxed not olde vpon thee, neither did thy foote swell those fourtie yeeres.
Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
5 Knowe therefore in thine heart, that as a man nourtereth his sonne, so the Lord thy God nourtereth thee.
Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
6 Therefore shalt thou keepe the commandements of the Lord thy God, that thou mayest walke in his wayes, and feare him.
Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
7 For the Lord thy God bringeth thee into a good land, a land in the which are riuers of water and fountaines, and depthes that spring out of valleis and mountaines:
Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
8 A land of wheate and barley, and of vineyards, and figtrees, and pomegranates: a land of oyle oliue and hony:
dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
9 A land wherein thou shalt eate bread without scarcitie, neither shalt thou lacke any thing therein: a land whose stones are yron, and out of whose mountaines thou shalt digge brasse.
dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
10 And when thou hast eaten and filled thy selfe, thou shalt blesse the Lord thy God for the good land, which he hath giuen thee.
Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
11 Beware that thou forget not the Lord thy God, not keeping his commandements, and his lawes, and his ordinances, which I commaund thee this day:
Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
12 Lest when thou hast eaten and filled thy selfe, and hast built goodly houses and dwelt therein,
kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
13 And thy beastes, and thy sheepe are increased, and thy siluer and golde is multiplied, and all that thou hast is increased,
ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
14 Then thine heart be lifted vp and thou forget the Lord thy God, which brought thee out of the land of Egypt, from the house of bondage,
mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
15 Who was thy guide in the great and terrible wildernes (wherein were fierie serpents, and scorpions, and drought, where was no water, who brought forth water for thee out of ye rock of flint:
Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
16 Who fed thee in the wildernesse with MAN, which thy fathers knewe not) to humble thee, and and to proue thee, that he might doe thee good at thy latter ende.
Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
17 Beware least thou say in thine heart, My power, and the strength of mine owne hand hath prepared me this abundance.
Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
18 But remember the Lord thy God: for it is he which giueth thee power to get substance to establish his couenant which he sware vnto thy fathers, as appeareth this day.
Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
19 And if thou forget the Lord thy God, and walke after other gods, and serue them, and worship them, I testifie vnto you this day that ye shall surely perish.
Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
20 As the nations which the Lord destroyeth before you, so ye shall perish, because ye woulde not be obedient vnto the voyce of the Lord your God.
Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.

< Deuteronomy 8 >