< Deuteronomy 7 >

1 When the Lord thy God shall bring thee into the land whither thou goest to possesse it, and shall roote out many nations before thee: the Hittites, and the Girgashites, and the Amorites, and the Canaanites, and the Perizzites, and the Hiuites, and the Iebusites, seuen nations greater and mightier then thou,
Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
2 And the Lord thy God shall giue them before thee, then thou shalt smite them: thou shalt vtterly destroy them: thou shalt make no couenant with them, nor haue compassion on them,
Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
3 Neither shalt thou make marriages with them, neither giue thy daughter vnto his sonne, nor take his daughter vnto thy sonne.
Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
4 For they wil cause thy sonne to turne away from me, and to serue other gods: then will the wrath of the Lord waxe hote against you and destroy thee suddenly.
Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
5 But thus ye shall deale with them, Ye shall ouerthrowe their altars, and breake downe their pillars, and ye shall cut downe their groues, and burne their grauen images with fire.
Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
6 For thou art an holy people vnto the Lord thy God, the Lord thy God hath chosen thee, to be a precious people vnto himselfe, aboue all people that are vpon the earth.
Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
7 The Lord did not set his loue vpon you, nor chose you, because ye were more in number then any people: for ye were the fewest of all people:
Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
8 But because the Lord loued you, and because hee would keepe the othe which hee had sworne vnto your fathers, the Lord hath brought you out by a mightie hand, and deliuered you out of the house of bondage from the hand of Pharaoh King of Egypt,
Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
9 That thou mayest knowe, that the Lord thy God, he is God, the faithfull God which keepeth couenant and mercie vnto them that loue him and keepe his commandements, euen to a thousand generations,
Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
10 And rewardeth them to their face that hate him, to bring them to destruction: he wil not deferre to reward him that hateth him, to his face.
Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
11 Keepe thou therefore the commandements, and the ordinances, and the lawes, which I commaund thee this day to doe them.
Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
12 For if ye hearken vnto these lawes, and obserue and doe them, then the Lord thy God shall keepe with thee the couenant, and the mercie which he sware vnto thy fathers.
Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
13 And he wil loue thee, and blesse thee, and multiplie thee: he will also blesse the fruite of thy wombe, and the fruite of thy land, thy corne and thy wine, and thine oyle and the increase of thy kine, and the flockes of thy sheepe in the land, which he sware vnto thy fathers to giue thee.
Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
14 Thou shalt be blessed aboue all people: there shall be neither male nor female barren among you, nor among your cattell.
Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
15 Moreouer, the Lord will take away from thee all infirmities, and will put none of the euill diseases of Egypt (which thou knowest) vpon thee, but wil send them vpon all that hate thee.
Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
16 Thou shalt therefore consume all people which the Lord thy God shall giue thee: thine eye shall not spare them, neither shalt thou serue their gods, for that shalbe thy destruction.
Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
17 If thou say in thine heart, These nations are moe then I, how can I cast them out?
Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
18 Thou shalt not feare them, but remember what the Lord thy God did vnto Pharaoh, and vnto all Egypt:
Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
19 The great tentations which thine eyes sawe, and the signes and wonders, and the mighty hand and stretched out arme, whereby the Lord thy God brought thee out: so shall the Lord thy God do vnto all ye people, whose face thou fearest.
Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
20 Moreouer, the Lord thy God will send hornets among them vntil they that are left, and hide themselues from thee, be destroyed.
Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
21 Thou shalt not feare them: for the Lord thy God is among you, a God mightie and dreadful.
Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
22 And the Lord thy God wil roote out these nations before thee by little and little: thou mayest not consume them at once, least the beasts of the fielde increase vpon thee.
Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
23 But the Lord thy God shall giue them before thee, and shall destroy them with a mightie destruction, vntill they be brought to naught.
Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
24 And he shall deliuer their Kings into thine hand, and thou shalt destroy their name from vnder heauen: there shall no man be able to stand before thee, vntill thou hast destroyed them.
Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
25 The grauen images of their gods shall ye burne with fire, and couet not the siluer and golde, that is on them, nor take it vnto thee, least thou be snared therewith: for it is an abomination before the Lord thy God.
Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
26 Bring not therefore abomination into thine house, lest, thou be accursed like it, but vtterly abhorre it, and count it most abominable: for it is accursed.
Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.

< Deuteronomy 7 >