< Deuteronomy 5 >

1 Then Moses called all Israiel, and saide vnto them, Heare, O Israel, the ordinances and the lawes which I propose to you this day, that yee may learne them, and take heede to obserue them.
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati: Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata.
2 The Lord our God made a couenant with vs in Horeb.
Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu.
3 The Lord made not this couenant with our fathers onely, but with vs, euen with vs all here aliue this day.
Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero.
4 The Lord talked with you face to face in the Mount, out of the middes of the fire.
Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja.
5 (At that time I stoode betweene the Lord and you, to declare vnto you ye word of the Lord: for ye were afraid at the sight of the fire, and went not vp into the mount, and he said,
(Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:
6 I am the Lord thy God, which haue brought thee out of the lande of Egypt, from the house of bondage.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
7 Thou shalt haue none other gods before my face.
“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.
8 Thou shalt make thee no grauen image or any likenesse of that that is in heauen aboue, or which is in the earth beneath, or that is in the waters vnder the earth.
“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
9 Thou shalt neither bowe thy selfe vnto them, nor serue them: for I the Lord thy God am a ielous God, visiting the iniquitie of the fathers vpon the children, euen vnto the third and fourth generation of them that hate me:
Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane,
10 And shewing mercie vnto thousandes of them that loue me, and keepe my commandements.
koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.
11 Thou shalt not take the Name of the Lord thy God in vaine: for the Lord will not holde him giltlesse that taketh his Name in vaine.
“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
12 Keepe the Sabbath day, to sanctifie it, as the Lord thy God hath commanded thee.
“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira.
13 Sixe dayes thou shalt labour, and shalt doe all thy worke:
Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi,
14 But the seuenth day is the Sabbath of the Lord thy God: thou shalt not doe any worke therein, thou, nor thy sonne, nor thy daughter, nor thy man seruant, nor thy mayd, nor thine oxe, nor thine asse, neither any of thy cattel, nor the stranger that is within thy gates: that thy man seruant and thy mayde may rest aswell as thou.
koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo.
15 For, remember that thou wast a seruant in the land of Egypt, and that the Lord thy God brought thee out thence by a mightie hand and a stretched out arme: therefore the Lord thy God commanded thee to obserue the Sabbath day.
Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.
16 Honour thy father and thy mother, as the Lord thy God hath comanded thee, that thy dayes may be prolonged, and that it may go well with thee vpon the land, which the Lord thy God giueth thee.
“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
17 Thou shalt not kill.
“Usaphe.
18 Neither shalt thou commit adulterie.
“Usachite chigololo.
19 Neither shalt thou steale.
“Usabe.
20 Neither shalt thou beare false witnesse against thy neighbour.
“Usapereke umboni womunamizira mnzako.
21 Neither shalt thou couet thy neighbours wife, neither shalt thou desire thy neighbours house, his fielde, nor his man seruant, nor his mayd, his oxe, nor his asse, nor ought that thy neighbour hath.
“Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
22 These wordes the Lord spake vnto all your multitude in the mount out of the mids of the fire, the cloude and the darkenes, with a great voyce, and added no more thereto: and wrote them vpon two tables of stone, and deliuered them vnto me.
Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.
23 And when ye heard the voyce out of the middes of the darkenes, (for the mountaine did burne with fire) then ye came to me, all the chiefe of your tribes, and your Elders:
Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine.
24 And ye sayd, Beholde, the Lord our God hath shewed vs his glory and his greatnes, and we haue heard his voyce out of the middes of the fire: we haue seene this day that God doeth talke with man, and he liueth.
Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye.
25 Now therefore, why should we dye? for this great fire wil consume vs: if we heare ye voyce of the Lord our God any more, we shall dye.
Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu.
26 For what flesh was there euer, that heard the voyce of the liuing God speaking out of the middes of the fire as we haue, and liued?
Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo?
27 Go thou neere and heare all that the Lord our God saith: and declare thou vnto vs all that the Lord our God saith vnto thee, and we will heare it, and doe it.
Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”
28 Then the Lord heard the voyce of your wordes, when ye spake vnto me: and the Lord sayd vnto me, I haue heard the voyce of ye wordes of this people, which they haue spoken vnto thee: they haue well sayd, all that they haue spoken.
Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino.
29 Oh that there were such an heart in them to feare me, and to keepe all my commandements alway: that it might go well with them, and with their children for euer.
Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.
30 Go, say vnto them, Returne you into your tentes.
“Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo.
31 But stand thou here with me, and I wil tell thee all the commandements, and the ordinances, and the lawes, which thou shalt teach them: that they may doe them in the land which I giue them to possesse it.
Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”
32 Take heede therefore, that ye doe as the Lord your God hath commanded you: turne not aside to the right hand nor to the left,
Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.
33 But walke in all the wayes which the Lord your God hath commanded you, that ye may liue, and that it may goe well with you: and that ye may prolong your dayes in the land which ye shall possesse.
Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.

< Deuteronomy 5 >