< Deuteronomy 23 >
1 None that is hurt by bursting, or that hath his priuie member cut off, shall enter into the Congregation of the Lord.
Mwamuna aliyense wofulidwa kapena woduka chiwalo chachimuna asalowe nawo mu msonkhano wa Yehova.
2 A bastard shall not enter into the Congregation of the Lord: euen to his tenth generation shall he not enter into the Congregation of the Lord.
Aliyense wobadwa mʼbanja losavomerezeka, kapena mdzukulu wake wina aliyense, ngakhale mibado khumi pambuyo pake, asalowe mu msonkhano wa Yehova.
3 The Ammonites and the Moabites shall not enter into the Congregation of the Lord: euen to their tenth generation shall they not enter into the Congregation of the Lord for euer,
Mwamoni kapena Mmowabu asalowe mu msonkhano wa anthu a Yehova ngakhale mibado khumi yobwera pambuyo pake.
4 Because they met you not with bread and water in the way, when yee came out of Egypt, and because they hyred against thee Balaam the sonne of Beor, of Pethor in Aram-naharaim, to curse thee.
Pakuti iwowa sanabwere kudzakulonjerani ndi chakudya kapena madzi pamene mumadutsa pochokera ku Igupto, mʼmalo mwake anakalemba ganyu Balaamu mwana wa Beori wochokera ku Petori ku Mesopotamiya kuti akutemberereni.
5 Neuerthelesse, the Lord thy God would not hearken vnto Balaam, but the Lord thy God turned the curse to a blessing vnto thee, because the Lord thy God loued thee.
Komabe Yehova Mulungu wanu sanamvere Balaamu koma anatembenuza temberero kukhala dalitso kwa inu chifukwa Yehova Mulungu wanu amakukondani.
6 Thou shalt not seeke their peace nor their prosperitie all thy dayes for euer.
Musachite nawo mgwirizano uliwonse wa mtendere pa moyo wanu wonse.
7 Thou shalt not abhorre an Edomite: for he is thy brother, neither shalt thou abhorre an Egyptian, because thou wast a strager in his land.
Musapeputse Mwedomu pakuti ndi mʼbale wanu ndithu. Musapeputse Mwigupto chifukwa munali alendo mʼdziko lake.
8 The children that are begotten of them in their thirde generation, shall enter into the Congregation of the Lord.
Mʼbado wachitatu wa ana awo akhoza kulowa mu msonkhano wa anthu a Yehova.
9 When thou goest out with the host against thine enemies, keepe thee then from all wickednesse.
Mukamakhala pa msasa pokonzekera adani anu, musayandikane ndi china chilichonse chodetsedwa.
10 If there be among you any that is vncleane by that which commeth to him by night, he shall goe out of the hoste, and shall not enter into the hoste,
Wina mwa asilikali anu akadziwonongera ndi umuna usiku, ayenera kuchoka pa msasapo ndipo akhale kunja kwa msasa.
11 But at euen he shall wash him selfe with water, and when the sunne is downe, he shall enter into the hoste.
Koma dzuwa likapendeka ayenera kusamba ndipo polowa dzuwa akhoza kubwerera ku msasa.
12 Thou shalt haue a place also without the hoste whither thou shalt resort,
Mukonze malo kunja kwa msasa kumene mukhoza kukadzithandizirako.
13 And thou shalt haue a paddle among thy weapons, and when thou wouldest sit downe without, thou shalt shalt digge therewith, and returning thou shalt couer thine excrements.
Pakati pa zida zanu muzikhala ndi china chokumbira, ndipo pokadzithandiza muzikumba kadzenje ndi kukwirira chimbudzi chanu.
14 For the Lord thy God walketh in the mids of thy campe to deliuer thee, and to giue thee thine enemies before thee: therefore thine hoste shalbe holy, that he see no filthie thing in thee and turne away from thee.
Pakuti Yehova Mulungu wanu amayendayenda ku msasa wanu kukutchinjirizani ndi kupereka adani anu kwa inu. Nʼchifukwa chake msasa wanu uzikhala wopatulika kuti mwina angaone china chonyansa nabwerera osakuyandikirani.
15 Thou shalt not deliuer the seruant vnto his master, which is escaped from his master vnto thee.
Ngati kapolo wathawa mbuye wake nakabisala kwanu, musamuperekenso kwa mbuye wakeyo.
16 He shall dwell with thee, euen among you, in what place he shall chuse, in one of thy cities where it liketh him best: thou shalt not vexe him.
Mumulole akhale pakati panu, paliponse pamene angakonde, mʼmudzi umene angasankhe ndipo musamupondereze.
17 There shalbe no whore of the daughters of Israel, neither shall there be a whore keeper of the sonnes of Israel.
Pasapezeke Mwisraeli wamwamuna kapena wamkazi wochita chiwerewere ku Nyumba ya Mulungu.
18 Thou shalt neyther bring the hyre of a whore, nor the price of a dogge into the house of the Lord thy God for any vow: for euen both these are abomination vnto the Lord thy God.
Musabweretse malipiro a wachiwerewere wamkazi kapena wamwamuna Mʼnyumba ya Yehova Mulungu wanu kudzapereka za malumbiro aliwonse, chifukwa Yehova Mulungu wanu amadana ndi zimenezi.
19 Thou shalt not giue to vsurie to thy brother: as vsurie of money, vsurie of meate, vsurie of any thing that is put to vsurie.
Musamalipitse mʼbale wanu chiwongoladzanja, kaya pa ndalama, kapena pa chakudya, kapena pa china chilichonse choti nʼkupereketsa chiwongoladzanja.
20 Vnto a stranger thou mayest lend vpon vsurie, but thou shalt not lend vpon vsurie vnto thy brother, that the Lord thy God may blesse thee in all that thou settest thine hand to, in the land whither thou goest to possesse it.
Mlendo mukhoza kumulipitsa chiwongoladzanja koma osati mʼbale wanu Mwisraeli, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochitika zanu zonse mʼdziko mukulowamoli.
21 When thou shalt vowe a vowe vnto the Lord thy God, thou shalt not be slacke to paye it: for the Lord thy God will surely require it of thee, and so it should be sinne vnto thee.
Mukalumbira kupereka kanthu kwa Yehova Mulungu wanu, musamachedwetse kupereka, chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakufunsanibe kanthuko ndipo mudzapezeka wochimwa.
22 But when thou absteinest from vowing, it shalbe no sinne vnto thee.
Koma ngati mupewa kupanga mapangano simudzapezeka ochimwa.
23 That which is gone out of thy lippes, thou shalt keepe and performe, as thou hast vowed it willingly vnto the Lord thy God: for thou hast spoken it with thy mouth.
Zilizonse zimene mulumbira ndi pakamwa panu muzitsimikiza kuzichita, chifukwa mwalumbira mwaufulu pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi pakamwa panu.
24 When thou commest vnto thy neighbours vineyard, then thou mayest eate grapes at thy pleasure, as much as thou wilt: but thou shalt put none in thy vessell.
Mukalowa mʼmunda wamphesa wa mnzanu mukhoza kudya mphesa mmene mungafunire koma musayike zina mʼdengu mwanu.
25 When thou commest into thy neighbours corne thou mayest plucke the eares with thine hand, but thou shalt not moue a sickle to thy neighbours corne.
Mukalowa mʼmunda wa tirigu wa mʼbale wanu, mukhoza kutengako ngala mʼmanja mwanu, koma osasenga tirigu ndi chikwakwa.