< Deuteronomy 18 >

1 The Priests of the Leuites, and all the tribe of Leui shall haue no part nor inheritace with Israel, but shall eate the offerings of the Lord made by fire, and his inheritance.
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 Therefore shall they haue no inheritance among their brethren: for the Lord is their inheritance, as he hath sayd vnto them.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 And this shalbe the Priests duetie of the people, that they, which offer sacrifice, whether it be bullocke or sheepe, shall giue vnto the Priest the shoulder, and the two cheekes, and the mawe.
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 The first fruites also of thy corne, of thy wine, and of thine oyle, and the first of the fleece of thy sheepe shalt thou giue him.
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 For the Lord thy God hath chosen him out of all thy tribes, to stande and minister in the Name of the Lord, him, and his sonnes for euer.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 Also when a Leuite shall come out of any of thy cities of all Israel, where hee remained, and come with all the desire of his heart vnto the place, which the Lord shall chuse,
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 He shall then minister in the Name of the Lord his God, as all his brethren the Leuites, which remaine there before the Lord.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 They shall haue like portions to eat beside that which commeth of his sale of his patrimonie.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 When thou shalt come into ye land which the Lord thy God giueth thee, thou shalt not learne to do after ye abominations of those nations.
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 Let none be founde among you that maketh his sonne or his daughter to goe thorough the fire, or that vseth witchcraft, or a regarder of times, or a marker of the flying of foules, or a sorcerer,
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 Or a charmer, or that counselleth with spirits, or a soothsaier, or that asketh counsel at ye dead.
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 For all that doe such things are abomination vnto the Lord, and because of these abominations the Lord thy God doeth cast them out before thee.
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 Thou shalt be vpright therefore with the Lord thy God.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 For these nations which thou shalt possesse, hearken vnto those that regarde the times, and vnto sorcerers: as for thee, the Lord thy God hath not suffred thee so.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 The Lord thy God will raise vp vnto thee a Prophet like vnto me, from among you, euen of thy brethren: vnto him ye shall hearken,
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 According to al that thou desiredst of the Lord thy God in Horeb, in the day of the assemblie, when thou saidest, Let me heare the voice of my Lord God no more, nor see this great fire any more, that I die not.
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 And the Lord sayde vnto me, They haue well spoken.
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 I will raise them vp a Prophet from among their brethren like vnto thee, and will put my woordes in his mouth, and he shall speake vnto them all that I shall commaund him.
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 And whosoeuer will not hearken vnto my wordes, which he shall speake in my Name, I will require it of him.
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 But the prophet that shall presume to speake a worde in my name, which I haue not commanded him to speake, or that speaketh in the name of other gods, euen the same prophet shall die.
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 And if thou thinke in thine heart, Howe shall we knowe the worde which the Lord hath not spoken?
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 When a prophet speaketh in the Name of the Lord, if the thing follow not nor come to passe, that is the thing which the Lord hath not spoken, but the prophet hath spoken it presumptuously: thou shalt not therefore be afraid of him.
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Deuteronomy 18 >