< Daniel 6 >
1 It pleased Darius to set ouer the kingdome an hundreth and twentie gouernours, which should be ouer the whole kingdome,
Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
2 And ouer these, three rulers (of whome Daniel was one) that the gouernours might giue accompts vnto them, and the King should haue no domage.
ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
3 Now this Daniel was preferred aboue the rulers and gouernours, because the spirit was excellent in him, and the King thought to set him ouer the whole realme.
Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
4 Wherefore the rulers and gouernours sought an occasion against Daniel concerning the kingdome: but they could finde none occasion nor fault: for he was so faithfull that there was no blame nor fault found in him.
Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
5 Then sayd these men, We shall not finde an occasion against this Daniel, except we finde it against him concerning the Law of his God.
Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
6 Therefore the rulers and these gouernours went together to the King, and sayde thus vnto him, King Darius, liue for euer.
Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
7 All the rulers of thy kingdome, the officers and gouernours, the counsellers, and dukes haue consulted together to make a decree for the King and to establish a statute, that whosoeuer shall aske a petition of any god or man for thirtie dayes saue of thee, O King, he shalbe cast into the denne of lyons.
Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
8 Nowe, O King, confirme the decree, and seale the writing, that it be not changed according to the law of the Medes and Persians, which altereth not.
Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
9 Wherefore King Darius sealed the writing and the decree.
Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
10 Now when Daniel vnderstood that he had sealed the writing, hee went into his house, and his window being open in his chamber toward Ierusalem, he kneeled vpon his knees three times a day, and prayed and praysed his God, as he did aforetime.
Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
11 Then these men assembled, and founde Daniel praying, and making supplication vnto his God.
Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
12 So they came and, spake vnto the King concerning the Kings decree, Hast thou not sealed the decree, that euery man that shall make a request to any god or man within thirtie dayes, saue to thee, O King, shall be cast into the denne of lyons? The King answered, and sayd, The thing is true, according to the Lawe of the Medes and Persians, which altereth not.
Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
13 Then answered they, and sayd vnto the King, This Daniel which is of the children of the captiuitie of Iudah, regardeth not thee, O King, nor the decree, that thou hast sealed, but maketh his petition three times a day.
Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
14 When the King heard these wordes, hee was sore displeased with himselfe, and set his heart on Daniel, to deliuer him: and he laboured till the sunne went downe, to deliuer him.
Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
15 Then these men assembled vnto the King, and sayde vnto ye King, Vnderstand, O King, that the lawe of the Medes and Persians is, that no decree nor statute which the King confirmeth, may be altered.
Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
16 Then the King commanded, and they brought Daniel, and cast him into the denne of lyons: now the King spake, and said vnto Daniel, Thy God, whome thou alway seruest, euen he will deliuer thee.
Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
17 And a stone was brought, and layed vpon the mouth of the denne, and the King sealed it with his owne signet, and with the signet of his princes, that the purpose might not be changed, concerning Daniel.
Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
18 Then the King went vnto his palace, and remained fasting, neither were the instruments of musike brought before him, and his sleepe went from him.
Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
19 Then the King arose early in the morning, and went in all haste vnto the denne of lyons.
Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
20 And when he came to the denne, he cryed with a lamentable voyce vnto Daniel: and the King spake, and saide to Daniel, O Daniel, the seruant of ye liuing God, is not thy God (whom thou alway seruest) able to deliuer thee from the lyons?
Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
21 Then saide Daniel vnto the King, O King, liue for euer.
Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
22 My God hath sent his Angel and hath shut the lyons mouthes, that they haue not hurt mee: for my iustice was founde out before him: and vnto thee, O King, I haue done no hurt.
Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
23 Then was the King exceeding glad for him, and commanded that they should take Daniel out of the denne: so Daniel was brought out of the denne, and no maner of hurt was found vpon him, because he beleeued in his God.
Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
24 And by the commandement of the King these me which had accused Daniel, were brought, and were cast into the denne of lions, euen they, their children, and their wiues: and the lyons had the mastry of them, and brake all their bones a pieces, or euer they came at the groud of the denne.
Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
25 Afterwarde King Darius wrote, Vnto all people, nations and languages, that dwel in all the world: Peace be multiplied vnto you.
Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
26 I make a decree that in all the dominion of my kingdome, men tremble and feare before the God of Daniel: for he is the liuing God, and remayneth for euer: and his kingdome shall not perish, and his dominion shalbe euerlasting.
“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
27 Hee rescueth and deliuereth, and hee worketh signes and wonders in heauen and in earth, who hath deliuered Daniel from the power of the lyons.
Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
28 So this Daniel prospered in the reigne of Darius and in the reigne of Cyrus of Persia.
Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.