< Daniel 4 >

1 Nebuchad-nezzar King vnto all people, nations and languages, that dwell in all the world, Peace be multiplied vnto you:
Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
2 I thought it good to declare the signes and wonders, that the hie God hath wrought toward me.
Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
3 How great are his signes, and how mightie are his wonders! his kingdome is an euerlasting kingdome, and his dominion is from generation to generation.
Zizindikiro zake ndi zazikulu,
4 I Nebuchad-nezzar being at rest in mine house, and flourishing in my palace,
Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
5 Saw a dreame, which made me afraide, and the thoughtes vpon my bed, and the visions of mine head troubled me.
Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
6 Therefore made I a decree, that they should bring all the wise men of Babel before mee, that they might declare vnto me the interpretation of the dreame.
Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
7 So came the inchanters, the astrologians, the Caldeans and the sothsayers, to whom I tolde the dreame, but they could not shew me the interpretation thereof,
Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
8 Till at the last Daniel came before mee, (whose name was Belteshazzar, according to the name of my god, which hath the spirite of the holy gods in him) and before him I tolde the dreame, saying,
Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
9 O Belteshazzar, chiefe of the enchanters, because I know, that the spirit of the holy gods is in thee, and no secret troubleth thee, tell mee the visions of my dreame, that I haue seene and the interpretation thereof.
Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
10 Thus were the visions of mine head in my bed. And beholde, I sawe a tree in the middes of the earth and the height thereof was great:
Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
11 A great tree and strong, and the height thereof reached vnto heauen, and the sight thereof to the endes of all the earth.
Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
12 The boughes thereof were faire and the fruite thereof much, and in it was meate for all: it made a shadow vnder it for the beastes of the fielde, and the foules of the heauen dwelt in the boughes thereof, and all flesh fedde of it.
Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
13 I sawe in the visions of mine head vpon my bed, and beholde, a watchman and an holy one came downe from heauen,
“Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
14 And cried aloude, and said thus, Hew downe the tree, and breake off his branches: shake off his leaues, and scatter his fruite, that the beastes may flee from vnder it, and the foules from his branches.
Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
15 Neuerthelesse leaue the stumpe of his rootes in the earth, and with a band of yron and brasse binde it among the grasse of the fielde, and let it be wet with the dewe of heauen, and let his portion be with the beastes among the grasse of the fielde.
Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
16 Let his heart be changed from mans nature, and let a beasts heart be giuen vnto him, and let seuen times be passed ouer him.
Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
17 The sentence is according to the decree of the watchmen, and according to the word of the holy ones: the demaunde was answered, to the intent that liuing men may knowe, that the most High hath power ouer the kingdome of men, and giueth it to whomsoeuer he will, and appointeth ouer it the most abiect among men.
“‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
18 This is the dreame, that I King Nebuchad-nezzar haue seene: therefore thou, O Belteshazzar, declare the interpretation thereof: for all the wisemen of my kingdome are not able to shewe mee the interpretation: but thou art able, for the spirit of the holy gods is in thee.
“Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
19 Then Daniel (whose name was Belteshazzar) held his peace by the space of one houre, and his thoughts troubled him, and the King spake and said, Belteshazzar, let neither the dreame, nor the interpretation thereof trouble thee. Belteshazzar answered and saide, My lord, the dreame be to them that hate thee, and the interpretation thereof to thine enemies.
Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
20 The tree that thou sawest, which was great and mightie, whose height reached vnto the heauen, and the sight thereof through all the world,
Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
21 Whose leaues were faire and the fruit thereof much, and in it was meate for all, vnder the which the beastes of the fielde dwelt, and vpon whose branches the foules of the heauen did sit,
mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
22 It is thou, O King, that art great and mightie: for thy greatnesse is growen, and reacheth vnto heauen, and thy dominion to the endes of the earth.
Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
23 Where as the King sawe a watchman, and an holy one, that came downe from heauen, and said, Hew downe the tree and destroy it, yet leaue the stumpe of the rootes thereof in the earth, and with a bande of yron and brasse binde it among the grasse of the fielde, and let it be wette with the dewe of heauen, and let his portion be with the beastes of the fielde, till seuen times passe ouer him,
“Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
24 This is the interpretation, O King, and it is the decree of the most High, which is come vpon my lord the King,
“Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
25 That they shall driue thee from men, and thy dwelling shalbe with the beasts of the fielde: they shall make thee to eate grasse as the oxen, and they shall wet thee with the dewe of heauen: and seuen times shall passe ouer thee, till thou knowe, that the most High beareth rule ouer the kingdome of men, and giueth it to whom so euer he will.
Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
26 Where as they sayd, that one should leaue the stumpe of the tree rootes, thy kingdome shall remaine vnto thee: after that, thou shalt knowe, that the heauens haue the rule.
Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
27 Wherefore, O King, let my counsell be acceptable vnto thee, and breake off thy sinnes by righteousnes, and thine iniquities by mercy toward the poore: lo, let there be an healing of thine errour.
Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
28 All these things shall come vpon the King Nebuchad-nezzar.
Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
29 At the end of twelue moneths, he walked in the royall palace of Babel.
Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
30 And the King spake and sayde, Is not this great Babel, that I haue built for the house of the kingdome by the might of my power, and for the honour of my maiestie?
iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
31 While the worde was in the Kings mouth, a voyce came downe from heauen, saying, O King Nebuchad-nezzar, to thee be it spoken, Thy kingdome is departed from thee,
Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
32 And they shall driue thee from men, and thy dwelling shalbe with the beastes of the fielde: they shall make thee to eate grasse, as the oxen, and seuen times shall passe ouer thee, vntill thou knowest, that the most High beareth rule ouer the kingdome of men, and giueth it vnto whomsoeuer he will.
Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
33 The very same houre was this thing fulfilled vpon Nebuchad-nezzar, and hee was driuen from men, and did eate grasse as the oxen, and his body was wet with the dewe of heauen, till his heares were growen as eagles feathers, and his nailes like birds clawes.
Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
34 And at the ende of these dayes I Nebuchad-nezzar lift vp mine eyes vnto heauen, and mine vnderstanding was restored vnto me, and I gaue thankes vnto the most High, and I praysed and honoured him that liueth for euer, whose power is an euerlasting power, and his kingdome is from generation to generation.
Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
35 And all the inhabitants of the earth are reputed as nothing: and according to his will he worketh in the armie of heauen, and in the inhabitants of the earth: and none can stay his hand, nor say vnto him, What doest thou?
Anthu onse a dziko lapansi
36 At the same time was mine vnderstanding restored vnto me, and I returned to the honour of my kingdome: my glory and my beautie was restored vnto me, and my counsellours and my princes sought vnto me, and I was established in my kingdome, and my glory was augmented toward me.
Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
37 Now therefore I Nebuchad-nezzar prayse and extoll and magnifie the King of heauen, whose workes are all trueth, and his wayes iudgement, and those that walke in pride, he is able to abase.
Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.

< Daniel 4 >