< Amos 9 >
1 I sawe the Lord standing vpon the altar, and he sayde, Smite the lintel of the doore, that the postes may shake: and cut them in pieces, euen the heads of them all, and I will slay the last of them with the sword: he that fleeth of them, shall not flee away: and he that escapeth of them, shall not be deliuered.
Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
2 Though they digge into the hell, thence shall mine hande take them: though they clime vp to heauen, thence will I bring them downe. (Sheol )
Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol )
3 And though they hide them selues in the toppe of Carmel, I will search and take them out thence: and though they be hid from my sight in the bottome of the sea, thence will I commande the serpent, and he shall bite them.
Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
4 And though they goe into captiuitie before their enemies, thence wil I commande the sword, and it shall slay them: and I will set mine eyes vpon them for euill, and not for good.
Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
5 And the Lord God of hosts shall touch the land, and it shall melt away, and al that dwel therein shall mourne, and it shall rise vp wholy like a flood, and shall bee drowned as by the flood of Egypt.
Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
6 He buildeth his spheres in the heauen, and hath laide the foundation of his globe of elements in the earth: hee calleth the waters of the sea, and powreth them out vpon the open earth: the Lord is his Name.
Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
7 Are ye not as the Ethiopians vnto mee, O children of Israel, sayeth the Lord? haue not I brought vp Israel out of the land of Egypt? and the Philistims from Caphtor, and Aram from Kir?
“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
8 Beholde, the eyes of the Lord God are vpon the sinfull kingdome, and I will destroy it cleane out of the earth. Neuerthelesse I will not vtterly destroy the house of Iaakob, saith the Lord.
“Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
9 For loe, I will command and I will sift the house of Israel among all nations, like as corne is sifted in a sieue: yet shall not the least stone fall vpon the earth.
“Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
10 But all the sinners of my people shall dye by the sword, which say, The euill shall not come, nor hasten for vs.
Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
11 In that day will I raise vp the tabernacle of Dauid, that is fallen downe, and close vp the breaches therof, and I will rayse vp his ruines, and I will builde it, as in the dayes of olde,
“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
12 That they may possesse the remnant of Edom, and of all the heathen, because my Name is called vpon them, sayeth the Lord, that doeth this.
kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
13 Behold, the dayes come, saith the Lord, that the plowman shall touche the mower, and the treader of grapes him that soweth seede: and the mountaines shall drop sweete wine, and all the hilles shall melt.
Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
14 And I will bring againe the captiuitie of my people of Israel: and they shall build the waste cities, and inhabite the, and they shall plant vineyardes, and drinke the wine thereof: they shall also make gardens, and eate the fruites of them.
Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
15 And I wil plant them vpon their land, and they shall no more bee pulled vp againe out of their lande, which I haue giuen them, sayeth the Lord thy God.
Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.