< Amos 7 >

1 Thus hath the Lord God shewed vnto mee, and beholde, he formed grashoppers in the beginning of ye shooting vp of the latter grouth: and loe, it was in the latter grouth after the Kings mowing.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 And when they had made an ende of eating the grasse of the land, then I saide, O Lord God, spare, I beseeche thee: who shall raise vp Iaakob? for he is small.
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 So the Lord repented for this. It shall not be, saith the Lord.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Thus also hath the Lord God shewed vnto me, and behold, the Lord God called to iudgement by fire, and it deuoured the great deepe, and did eate vp a part.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Then said I, O Lord God, cease, I beseeche thee: who shall raise vp Iaakob? for he is small.
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 So the Lord repented for this. This also shall not be, saith the Lord God.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Thus againe he shewed me, and behold, the Lord stoode vpon a wall made by line with a line in his hand.
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 And the Lord saide vnto me, Amos, what seest thou? And I said, A line. Then said the Lord, Beholde, I wil set a line in the middes of my people Israel, and wil passe by them no more.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 And the hye places of Izhak shalbe desolate, and the temples of Israel shalbe destroyed: and I wil rise against the house of Ieroboam with the sworde.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Then Amaziah the Priest of Beth-el sent to Ieroboam King of Israel, saying, Amos hath conspired against thee in the middes of the house of Israel: the lande is not able to beare all his wordes.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 For thus Amos saith, Ieroboam shall die by the sworde, and Israel shalbe led away captiue out of their owne land.
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 Also Amaziah sayde vnto Amos, O thou the Seer, goe, flee thou away into the land of Iudah, and there eate thy bread and prophecie there.
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 But prophecie no more at Beth-el: for it is the Kings chappel, and it is the Kings court.
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Then answered Amos, and said to Amaziah, I was no Prophet, neither was I a prophets sonne, but I was an herdman, and a gatherer of wilde figs.
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 And the Lord tooke me as I followed the flocke, and the Lord said vnto me, Go, prophecie vnto my people Israel.
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Now therefore heare thou the word of the Lord. Thou sayest, Prophecie not against Israel, and speake nothing against the house of Izhak.
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 Therefore thus sayth the Lord, Thy wife shall be an harlot in the citie, and thy sonnes and thy daughters shall fall by the sword, and thy land shall be deuided by line: and thou shalt die in a polluted land, and Israel shall surely go into captiuitie forth of his land.
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Amos 7 >