< Amos 5 >

1 Heare ye this worde, which I lift vp vpon you, euen a lamentation of the house of Israel.
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 The virgine Israel is fallen, and shall no more rise: shee is left vpon her lande, and there is none to raise her vp.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 For thus saith ye Lord God, The citie which went out by a thousand, shall leaue an hundreth: and that which went forth by an hundreth, shall leaue ten to the house of Israel.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 For thus saith the Lord vnto the house of Israel, Seeke ye me, and ye shall liue.
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 But seeke not Beth-el, nor enter into Gilgal, and go not to Beer-sheba: for Gilgal shall goe into captiuitie, and Beth-el shall come to nought.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Seeke the Lord, and yee shall liue, least he breake out like fire in the house of Ioseph and deuoure it, and there be none to quench it in Beth-el.
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 They turne iudgement to wormewood, and leaue off righteousnes in the earth.
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 He maketh Pleiades, and Orion, and he turneth the shadowe of death into the morning, and he maketh the day darke as night: he calleth the waters of the sea, and powreth them out vpon the open earth: the Lord is his Name.
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 He strengtheneth the destroyer against the mightie: and the destroyer shall come against the fortresse.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 They haue hated him, that rebuked in the gate: and they abhorred him that speaketh vprightly.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 Forasmuch then as your treading is vpon the poore, and yee take from him burdens of wheate, ye haue built houses of hewen stone, but ye shall not dwel in them: ye haue plated pleasant vineyards, but ye shall not drinke wine of them.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 For I know your manifold transgressions, and your mightie sinnes: they afflict the iust, they take rewards, and they oppresse the poore in ye gate.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Therefore the prudent shall keepe silence in that time, for it is an euill time.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Seeke good and not euil, that ye may liue: and the Lord God of hostes shalbe with you, as you haue spoken.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Hate the euil, and loue the good, and establish iudgement in the gate: it may bee that the Lord God of hostes will be mercifull vnto the remnant of Ioseph.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 Therfore the Lord God of hosts, the Lord saith thus, Mourning shalbe in all streetes: and they shall say in al the hie wayes, Alas, alas: and they shall call the husbandman to lamentation, and such as can mourne, to mourning.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 And in al the vines shalbe lamentation: for I wil passe through thee, saith the Lord.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Woe vnto you, that desire the day of the Lord: what haue you to do with it? the day of the Lord is darkenes and not light.
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 As if a man did flee from a lyon, and a beare met him: or went into the house, and leaned his hand on the wall, and a serpent bit him.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Shal not the day of the Lord be darkenes, and not light? euen darkenes and no light in it?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 I hate and abhorre your feast dayes, and I wil not smelll in your solemne assemblies.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Though ye offer me burnt offrings and meat offrings, I wil not accept them: neither will I regard the peace offrings of your fat beasts.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Take thou away from me the multitude of thy songs (for I wil not heare the melodie of thy violes)
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 And let iudgement runne downe as waters, and righteousnesse as a mightie riuer.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Haue ye offered vnto me sacrifices and offrings in the wildernesse fourtie yeeres, O house of Israel?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 But you haue borne Siccuth your King, and Chiun your images, and the starre of your gods, which ye made to your selues.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Therefore wil I cause you to goe into captiuitie beyond Damascus, saith the Lord, whose Name is the God of hostes.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amos 5 >