< Amos 2 >
1 Thus sayth the Lord, For three transgressions of Moab, and for foure, I will not turne to it, because it burnt the bones of the King of Edom into lime.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Therefore will I send a fire vpon Moab, and it shall deuoure the palaces of Kerioth, and Moab shall die with tumult, with shouting, and with the sound of a trumpet.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 And I will cut off the iudge out of the mids thereof, and will slay all the princes thereof with him, sayth the Lord.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Thus saith the Lord, For three transgressions of Iudah, and for foure, I will not turne to it, because they haue cast away the Lawe of the Lord, and haue not kept his commandementes, and their lies caused them to erre after the which their fathers haue walked.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 Therefore will I send a fire vpon Iudah, and it shall deuoure the palaces of Ierusalem.
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Thus sayth the Lord, For three transgressions of Israel, and for foure, I will not turne to it, because they solde the righteous for siluer and the poore for shooes.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 They gape ouer the head of the poore, in the dust of the earth, and peruert the wayes of the meeke: and a man and his father will goe in to a mayde to dishonour mine holy Name.
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 And they lye downe vpon clothes layde to pledge by euery altar: and they drinke the wine of the condemned in the house of their God.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Yet destroyed I the Amorite before the, whose height was like the height of the cedars, and he was strong as the okes: notwithstanding I destroyed his fruite from aboue, and his roote from beneath.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 Also I brought you vp from the land of Egypt, and led you fourtie yeres thorowe the wildernesse, to possesse the land of the Amorite.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 And I raysed vp of your sonnes for Prophets, and of your yong men for Nazarites. Is it not euen thus, O ye children of Israel, sayth the Lord?
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 But ye gaue the Nazarites wine to drinke, and commanded the Prophetes, saying, Prophecie not.
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Behold, I am pressed vnder you as a cart is pressed that is full of sheaues.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Therefore the flight shall perish from the swift, and the strong shall not strengthen his force, neither shall the mightie saue his life.
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 Nor he that handleth the bowe, shall stand, and he that is swift of foote, shall not escape, neyther shall he that rideth the horse, saue his life.
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 And he that is of a mighty courage among the strong men, shall flee away naked in that day, sayth the Lord.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.