< 2 Samuel 8 >

1 After this now, Dauid smote the Philistims, and subdued them, and Dauid tooke the bridle of bondage out of the hand of the Philistims.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 And hee smote Moab, and measured them with a corde, and cast them downe to the ground: he measured them with two cordes to put them to death, and with one full corde to keepe them aliue: so became the Moabites Dauids seruants, and brought giftes.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 Dauid smote also Hadadezer the sonne of Rehob King of Zobah, as he went to recouer his border at the riuer Euphrates.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 And Dauid tooke of them a thousand and seuen hundreth horsemen, and twenty thousande footemen, and Dauid destroyed all the charets, but he reserued an hundreth charets of them.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 Then came the Aramites of Dammesek to succour Hadadezer king of Zobah, but Dauid slewe of the Aramites two and twenty thousande men.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 And Dauid put a garison in Aram of Damesek: and the Aramites became seruants to Dauid, and brought gifts. And the Lord saued Dauid wheresoeuer he went.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 And Dauid tooke the shieldes of gold that beloged to the seruants of Hadadezer, and brought them to Ierusalem.
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 And out of Betah, and Berothai (cities of Hadadezer) king Dauid brought exceeding much brasse.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 Then Toi king of Hamath heard howe Dauid had smitten all the hoste of Hadadezer,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 Therefore Toi sent Ioram his sonne vnto King Dauid, to salute him, and to reioyce with him because he had fought against Hadadezer, and beaten him (for Hadadezer had warre with Toi) who brought with him vessels of siluer, and vessels of golde, and vessels of brasse.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 And King Dauid did dedicate them vnto the Lord with the siluer and golde that he had dedicate of all the nations, which he had subdued:
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
12 Of Aram, and of Moab, and of the children of Ammon, and of the Philistims, and of Amalek, and of the spoyle of Hadadezer ye sonne of Rehob King of Zobah.
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 So Dauid gate a name after that hee returned, and had slayne of the Aramites in the valley of salt eighteene thousand men.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 And he put a garison in Edom: throughout all Edom put he souldiers, and all they of Edom became Dauids seruants: and the Lord kept Dauid whithersoeuer he went.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 Thus Dauid reigned ouer all Israel, and executed iudgement and iustice vnto all his people.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 And Ioab the sonne of Zeruiah was ouer the hoste, and Ioshaphat the sonne of Ahilud was recorder.
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 And Zadok the sonne of Ahitub, and Ahimelech the sonne of Abiathar were the Priestes, and Seraiah the Scribe.
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 And Benaiah the sonne of Iehoiada and the Cherethites and the Pelethites, and Dauids sonnes were chiefe rulers.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.

< 2 Samuel 8 >