< 2 Samuel 7 >

1 Afterwarde when the King sate in his house and the Lord had giuen him rest rounde about from all his enemies,
Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
2 The King saide vnto Nathan the Prophet, Beholde, nowe I dwel in an house of cedar trees, and the Arke of God remayneth within the curtaines.
mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
3 Then Nathan sayde vnto the King, Go, and doe all that is in thine heart: for the Lord is with thee.
Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
4 And the same night the worde of the Lord came vnto Nathan, saying,
Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
5 Goe and tell my seruant Dauid, Thus saieth the Lord, Shalt thou buylde me an house for my dwelling?
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
6 For I haue dwelt in no house since the time that I brought the children of Israel out of Egypt vnto this day, but haue walked in a tent and tabernacle.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
7 In al the places wherein I haue walked with all the children of Israel, spake I one worde with any of the tribes of Israel when I commanded the iudges to feede my people Israel? or sayde I, Why build ye not me an house of cedar trees?
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
8 Nowe therefore so say vnto my seruant Dauid, Thus saieth the Lord of hostes, I tooke thee from the sheepecote following the sheepe, that thou mightest bee ruler ouer my people, ouer Israel.
“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
9 And I was with thee wheresoeuer thou hast walked, and haue destroyed all thine enemies out of thy sight, and haue made thee a great name, like vnto the name of the great men that are in the earth.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
10 (Also I will appoynt a place for my people Israel, and will plant it, that they may dwell in a place of their owne, and moue no more, neither shall wicked people trouble them any more as before time,
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
11 And since the time that I set Iudges ouer my people of Israel) and I will giue thee rest from al thine enemies: also the Lord telleth thee, that he will make thee an house.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
12 And when thy daies bee fulfilled, thou shalt sleepe with thy fathers, and I wil set vp thy seede after thee, which shall proceede out of thy body, and will stablish his kingdome.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
13 He shall buyld an house for my Name, and I will stablish ye throne of his kingdome for euer.
Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
14 I will be his father, and hee shall bee my sonne: and if he sinne, I will chasten him with the rod of men, and with the plagues of the children of men.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
15 But my mercy shall not depart away from him, as I tooke it from Saul whome I haue put away before thee.
Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
16 And thine house shall be stablished and thy kingdome for euer before thee, euen thy throne shalbe stablished for euer.
Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
17 According to all these wordes, and according to all this vision, Nathan spake thus vnto Dauid.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
18 Then King Dauid went in, and sate before the Lord, and sayde, Who am I, O Lord God, and what is mine house, that thou hast brought me hitherto?
Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
19 And this was yet a small thing in thy sight, O Lord God, therefore thou hast spoken also of thy seruants house for a great while: but doth this appertaine to man, O Lord God?
Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
20 And what can Dauid say more vnto thee? for thou, Lord God, knowest thy seruant.
Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
21 For thy words sake, and according to thine owne heart hast thou done all these great things, to make them knowen vnto thy seruant.
Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
22 Wherefore thou art great, O Lord God: for there is none like thee, neither is there any God besides thee, according to all that wee haue heard with our eares.
Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
23 And what one people in the earth is like thy people, like Israel? whose God went and redeemed them to himselfe, that they might be his people, and that hee might make him a name, and do for you great things, and terrible for thy land, O Lord, euen for thy people, whome thou redeemedst to thee out of Egypt, from the nations, and their gods?
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
24 For thou hast ordeyned to thy selfe thy people Israel to be thy people for euer: and thou Lord art become their God.
Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
25 Nowe therefore, O Lord God, confirme for euer the word that thou hast spoken concerning thy seruant and his house, and doe as thou hast sayde.
“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
26 And let thy Name bee magnified for euer by them that shall say, The Lord of hostes is the God ouer Israel: and let the house of thy seruant Dauid be stablished before thee.
kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
27 For thou, O Lord of hostes, God of Israel, hast reueiled vnto thy seruant, saying, I will build thee an house: therefore hath thy seruant bene bold to pray this prayer vnto thee.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
28 Therefore now, O Lord God, (for thou art God, and thy words be true, and thou hast tolde this goodnes vnto thy seruant)
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
29 Therefore nowe let it please thee to blesse the house of thy seruant, that it may continue for euer before thee: for thou, O Lord God, hast spoken it: and let the house of thy seruant be blessed for euer, with thy blessing.
Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< 2 Samuel 7 >