< 2 Samuel 4 >

1 And when Sauls sonne heard that Abner was dead in Hebron, then his handes were feeble, and all Israel was afraide,
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 And Sauls sonne had two men that were captaines of bandes: the one called Baanah, and the other called Rechab, the sonnes of Rimmon a Beerothite of the children of Beniamin. (for Beeroth was reckened to Beniamin,
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 Because the Beerothites fled to Gittaim, and soiourned there, vnto this day).
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 And Ionathan Sauls sonne had a sonne that was lame on his feete: he was fiue yere olde when the tydings came of Saul and Ionathan out of Israel: then his nourse tooke him, and fledde away. And as she made haste to flee, the childe fell, and beganne to halte, and his name was Mephibosheth.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 And the sonnes of Rimmon the Beerothite, Rechab and Baanah went and came in the heat of the day to the house of Ish-bosheth (who slept on a bed at noone)
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 And beholde, Rechab and Baanah his brother came into the middes of the house as they would haue wheate, and they smote him vnder the fift ryb, and fled.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 For when they came into the house, he slept on his bed in his bed chamber, and they smote him, and slewe him, and beheaded him, and tooke his head, and gate them away through the plaine all the night.
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 And they brought the head of Ish-bosheth vnto Dauid to Hebron, and saide to the King, Beholde the head of Ish-bosheth Sauls sonne thine enemie, who sought after thy life: and the Lord hath auenged my lorde the King this day of Saul, and of his seede.
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 Then Dauid answered Rechab and Baanah his brother, the sonnes of Rimmon the Beerothite, and saide vnto them, As the Lord liueth, who hath deliuered my soule out of al aduersity,
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 When one tolde me, and sayde that Saul was dead, (thinking to haue brought good tydings) I tooke him and slewe him in Ziklag, who thought that I woulde haue giuen him a rewarde for his tidings:
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 How much more, when wicked men haue slaine a righteous person in his owne house, and vpon his bed? shall I not now therfore require his blood at your hand, and take you from the earth?
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 Then Dauid commanded his yong men, and they slew them, and cut off their hands and their feete, and hanged them vp ouer the poole in Hebron: but they tooke the head of Ishbosheth, and buried it in the sepulchre of Abner in Hebron.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.

< 2 Samuel 4 >