< 2 Peter 1 >

1 Simon Peter a seruant and an Apostle of Iesus Christ, to you which haue obteined like precious faith with vs by the righteousnesse of our God and Sauiour Iesus Christ:
Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
2 Grace and peace be multiplied to you, through the acknowledging of God, and of Iesus our Lord,
Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
3 According as his diuine power hath giuen vnto vs all things that perteine vnto life and godlinesse, through the acknowledging of him that hath called vs vnto glory and vertue.
Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
4 Whereby most great and precious promises are giuen vnto vs, that by them ye should be partakers of the diuine nature, in that ye flee the corruption, which is in the worlde through lust.
Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
5 Therefore giue euen all diligence thereunto: ioyne moreouer vertue with your faith: and with vertue, knowledge:
Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
6 And with knowledge, temperance: and with temperance, patience: and with patience, godlines:
Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
7 And with godlines, brotherly kindnes: and with brotherly kindnes, loue.
Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
8 For if these things be among you, and abound, they will make you that ye neither shalbe idle, nor vnfruitfull in the acknowledging of our Lord Iesus Christ:
Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
9 For he that hath not these things, is blinde, and can not see farre off, and hath forgotten that he was purged from his olde sinnes.
Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
10 Wherefore, brethren, giue rather diligence to make your calling and election sure: for if ye doe these things, ye shall neuer fall.
Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
11 For by this meanes an entring shalbe ministred vnto you aboundantly into the euerlasting kingdome of our Lord and Sauiour Iesus Christ. (aiōnios g166)
Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios g166)
12 Wherefore, I will not be negligent to put you alwayes in remembrance of these things, though that ye haue knowledge, and be stablished in the present trueth.
Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
13 For I thinke it meete as long as I am in this tabernacle, to stirre you vp by putting you in remembrance,
Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
14 Seeing I knowe that the time is at hand that I must lay downe this my tabernacle, euen as our Lord Iesus Christ hath shewed me.
chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
15 I will endeuour therefore alwayes, that ye also may be able to haue remembrance of these things after my departing.
Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
16 For we followed not deceiuable fables when we opened vnto you the power, and comming of our Lord Iesus Christ, but with our eyes we saw his maiestie:
Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
17 For he receiued of God the Father honour and glory, when there came such a voyce to him from that excellent glory, This is my beloued Sonne, in whom I am well pleased.
Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
18 And this voyce we heard when it came from heauen, being with him in the Holy mount.
Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
19 We haue also a most sure worde of the Prophets, to the which ye doe well that yee take heede, as vnto a light that shineth in a darke place, vntill the day dawne, and the day starre arise in your hearts.
Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
20 So that yee first knowe this, that no prophecie of the Scripture is of any priuate interpretation.
Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
21 For the prophecie came not in olde time by the will of man: but holy men of God spake as they were moued by the holy Ghost.
Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.

< 2 Peter 1 >