< 2 Kings 6 >

1 And the children of the Prophets saide vnto Elisha, Behold, we pray thee, the place where we dwell with thee, is too litle for vs.
Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri.
2 Let vs nowe goe to Iorden, that we may take thence euery man a beame, and make vs a place to dwell in. And he answered, Goe.
Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.” Ndipo Elisa anati, “Pitani.”
3 And one said, Vouchsafe, I pray thee, to go with thy seruants, and he answered, I will goe.
Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.” Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.”
4 So he went with them, and when they came to Iorden, they cut downe wood.
Ndipo anapita nawo. Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo.
5 And as one was felling of a tree, the yron fell into the water: then he cryed, and said, Alas master, it was but borowed.
Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!”
6 And the man of God saide, Where fell it? And he shewed him the place. Then he cut downe a piece of wood, and cast in thither, and he caused the yron to swimme.
Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama.
7 Then he saide, Take it vp to thee. And he stretched out his hand, and tooke it.
Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga.
8 Then the King of Aram warred against Israel, and tooke counsell with his seruants, and said, In such and such a place shalbe my campe.
Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.”
9 Therefore the man of God sent vnto the King of Israel, saying, Beware thou goe not ouer to such a place: for there the Aramites are come downe.
Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.”
10 So the King of Israel sent to the place which the man of God tolde him, and warned him of, and saued himselfe from thence, not once, nor twise.
Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo.
11 And the heart of the King of Aram was troubled for this thing: therefore he called his seruants and saide vnto them, Will ye not shewe me, which of vs bewrayeth our counsel to the king of Israel?
Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?”
12 Then one of his seruants saide, None, my lorde, O King, but Elisha the Prophet that is in Israel, telleth the King of Israel, euen the wordes that thou speakest in thy priuie chamber.
Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.”
13 And he said, Goe, and espie where he is, that I may sende and fetch him. And one tolde him, saying, Beholde, he is in Dothan.
Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.”
14 So he sent thither horses, and charets, and a mightie hoste: and they came by night, and compassed the citie.
Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo.
15 And when the seruant of the man of God arose earely to goe out, beholde, an hoste compassed the citie with horses and charets. Then his seruant sayde vnto him, Alas master, howe shall we doe?
Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?”
16 And he answered, Feare not: for they that be with vs, are moe then they that be with them.
Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.”
17 Then Elisha prayed, and saide, Lord, I beseech thee, open his eyes, that he may see. And the Lord opened the eyes of the seruant, and he looked, and beholde, the mountaine was full of horses and charets of fyre round about Elisha.
Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa.
18 So they came downe to him, but Elisha prayed vnto the Lord, and said, Smite this people, I pray thee, with blindnesse. And he smote them with blindnes, according to the worde of Elisha.
Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa.
19 And Elisha said vnto them, This is not the way, neither is this the citie: follow me, and I will leade you to the man whome ye seeke. But he ledde them to Samaria.
Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya.
20 And when they were come to Samaria, Elisha saide, Lord, open their eyes that they may see. And the Lord opened their eyes, and they saw, and beholde, they were in the mids of Samaria.
Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya.
21 And the King of Israel sayde vnto Elisha when he sawe them, My father, shall I smite them, shall I smite them?
Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?”
22 And he answered, Thou shalt not smite them: doest thou not smite them that thou hast taken with thy sworde, and with thy bowe? but set bread and water before them, that they may eate and drinke and goe to their master.
Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.”
23 And he made great preparation for them: and when they had eaten and drunken, he sent them away: and they went to their master. So ye bands of Aram came no more into the land of Israel.
Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli.
24 But afterward Ben-hadad King of Aram gathered all his hoste, and went vp, and besieged Samaria.
Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya.
25 So there was a great famine in Samaria: for loe, they besieged it vntill an asses head was at foure score pieces of siluer, and the fourth part of a kab of doues doung at fiue pieces of siluer.
Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu.
26 And as the King of Israel was going vpon the wall, there cryed a woman vnto him, saying, Helpe, my lord, O King.
Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!”
27 And he said, Seeing the Lord doeth not succour thee, howe shoulde I helpe thee with the barne, or with the wine presse?
Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?”
28 Also the King said vnto her, What ayleth thee? And she answered, This woman sayde vnto me, Giue thy sonne, that we may eate him to day, and we will eate my sonne to morowe,
Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’
29 So we sod my sonne, and did eate him: and I saide to her the day after, Giue thy sonne, that we may eate him, but she hath hid her sonne.
Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.”
30 And when the King had heard the wordes of the woman, he rent his clothes, (and as he went vpon the wall, the people looked, and behold, he had sackecloth within vpon his flesh)
Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli.
31 And he saide, God doe so to me and more also, if the head of Elisha the sonne of Shaphat shall stande on him this day.
Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!”
32 (Nowe Elisha sate in his house, and the Elders sate with him.) And the King sent a man before him: but before the messenger came to him, he saide to the Elders, See ye not howe this murtherers sonne hath sent to take away mine head? take heede when the messenger commeth, and shut the doore and handle him roughly at the doore: is not the sounde of his masters feete behinde him?
Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?”
33 While he yet talked with them, beholde, the messenger came downe vnto him, and saide, Behold, this euill commeth of the Lord: should I attende on the Lord any longer?
Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”

< 2 Kings 6 >