< 2 Kings 4 >

1 And one of the wiues of the sonnes of the Prophets cryed vnto Elisha, saying, Thy seruant mine husband is dead, and thou knowest, that thy seruant did feare the Lord: and the creditour is come to take my two sonnes to bee his bondmen.
Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”
2 Then Elisha saide vnto her, What shall I do for thee? tell mee, what hast thou at home? And she sayd, Thine handmayd hath nothing at home, saue a pitcher of oyle.
Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?” Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”
3 And he sayde, Goe, and borowe thee vessels abroad of all thy neighbours, emptie vessels, and spare not.
Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa.
4 And when thou art come in, thou shalt shut the doore vpon thee and vpon thy sonnes, and powre out into all those vessels, and set aside those that are full.
Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”
5 So shee departed from him, and shut the doore vpon her, and vpon her sonnes. And they brought to her, and she powred out.
Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta.
6 And when the vessels were full, shee sayde vnto her sonne, Bring mee yet a vessel. And hee said vnto her, There is no moe vessels. And the oyle ceased.
Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.” Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.
7 Then shee came and tolde the man of God. And he saide, Goe, and sell the oyle, and pay them that thou art in debt vnto, and liue thou and thy children of the rest.
Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”
8 And on a time Elisha came to Shunem, and there a woman of great estimation constrained him to eate bread: and as he passed by, he turned in thither to eate bread.
Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya.
9 And she sayde vnto her husband, Beholde, I know now, that this is an holy man of God that passeth by vs continually.
Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu.
10 Let vs make him a litle chamber, I pray thee, with walles, and let vs set him there a bed, and a table, and a stoole, and a candlesticke, that hee may turne in thither when hee commeth to vs.
Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”
11 And on a day, hee came thither and turned into the chamber, and lay therein,
Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo.
12 And sayd to Gehazi his seruant, Call this Shunammite: and when hee called her, she stood before him.
Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa.
13 Then he sayd vnto him, Say vnto her now, Beholde, thou hast had all this great care for vs, what shall we doe for thee? Is there any thing to bee spoken for thee to the King or to the captaine of the hoste? And shee answered, I dwell among mine owne people.
Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’” Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”
14 Againe he sayde, What is then to be done for her? Then Gehazi answered, In deede she hath no sonne, and her husband is olde.
Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?” Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”
15 Then said he, Cal her. And hee called her, and shee stoode in the doore.
Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo.
16 And he said, At this time appointed, according to the time of life, thou shalt embrace a sonne. And she sayd, Oh my Lord, thou man of God, doe not lye vnto thine handmayd.
Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.” Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”
17 So the woman conceiued, and bare a sonne at that same season, according to the time of life, that Elisha had sayd vnto her.
Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.
18 And when the childe was growen, it fell on a day, that he went out to his father, and to the reapers.
Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu.
19 And he sayde to his father, Mine head, mine head. Who sayd to his seruant, Beare him to his mother.
Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!” Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.”
20 And hee tooke him and brought him to his mother, and hee sate on her knees till noone, and dyed.
Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira.
21 Then shee went vp, and layed him on the bed of the man of God, and shut the doore vpon him, and went out.
Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.
22 Then she called to her husband, and sayd, Send with me, I pray thee, one of the yong men and one of the asses: for I will haste to the man of God, and come againe.
Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”
23 And he sayd, Wherefore wilt thou goe to him to day? it is neither newe moone nor Sabbath day. And she answered, All shalbe well.
Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
24 Then she sadled an asse, and sayde to her seruant, Driue, and goe forward: staye not for me to get vp, except I bid thee.
Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.”
25 So she went, and came vnto the man of God to mount Carmel. And when the man of God sawe her ouer against him, he sayd to Gehazi his seruant, Beholde, the Shunammite.
Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli. Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo!
26 Runne nowe, I say, to meete her, and say vnto her, Art thou in health? is thine husband in health? and is the child in health? And she answered, We are in health.
Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
27 And when shee came to the man of God vnto the moutaine, she caught him by his feete: and Gehazi went to her, to thrust her away: but the man of God said, Let her alone: for her soule is vexed within her, and the Lord hath hid it from me, and hath not told it mee.
Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”
28 Then she said, Did I desire a sonne of my lord? did I not say, Deceiue me not?
Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”
29 Then he sayd to Gehazi, Gird thy loynes, and take my staffe in thine hand, and goe thy way: if thou meete any, salute him not: and if any salute thee, answere him not: and laye my staffe vpon the face of the childe.
Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”
30 And the mother of the childe sayde, As the Lord liueth, and as thy soule liueth, I will not leaue thee. Therefore he arose, and followed her.
Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.
31 But Gehazi was gone before them, and had layed the staffe vpon the face of the childe, but he neither spake nor heard: wherefore hee returned to meete him, and told him, saying, The childe is not waken.
Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”
32 Then came Elisha into the house, and beholde, the childe was dead, and layed vpon his bedde.
Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake.
33 He went in therefore, and shut the doore vpon them twayne, and prayed vnto the Lord.
Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova.
34 After he went vp, and lay vpon the child, and put his mouth on his mouth, and his eyes vpon his eies, and his hands vpon his handes, and stretched himselfe vpon him, and the flesh of the child waxed warme.
Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda.
35 And hee went from him, and walked vp and downe in the house, and went vp and spred himselfe vpon him: then the childe neesed seuen times, and opened his eyes.
Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.
36 Then he called Gehazi, and sayd, Call this Shunammite. So he called her, which came in vnto him. And he said vnto her, Take thy sonne.
Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.”
37 And she came, and fell at his feete, and bowed her selfe to the ground, and tooke vp her sonne, and went out.
Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.
38 Afterward Elisha returned to Gilgal, and a famine was in the land, and the children of the Prophets dwelt with him. And hee sayd vnto his seruant, Set on the great pot, and seethe pottage for the children of the Prophets.
Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”
39 And one went out into the fielde, to gather herbes, and founde, as it were, a wilde vine, and gathered thereof wilde gourdes his garment ful, and came and shred them into the pot of pottage: for they knew it not.
Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa.
40 So they powred out for the men to eate: and when they did eate of the pottage, they cryed out, and sayde, O thou man of God, death is in the pot: and they could not eate thereof.
Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.
41 Then he said, Bring meale. And hee cast it into the potte, and sayd, Powre out for the people, that they may eate: and there was none euill in the pot.
Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.
42 Then came a man from Baal-shalisha, and brought the man of God bread of the first fruits, euen twenty loaues of barley, and full eares of corne in the huske. And hee saide, Giue vnto the people, that they may eate.
Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”
43 And his seruant answered, How shoulde I set this before an hundreth men? He sayd againe, Giue it vnto the people, that they may eate: for thus sayth the Lord, They shall eate, and there shall remaine.
Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?” Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’”
44 So he set it before them, and they did eate, and left ouer, according to the word of the Lord.
Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.

< 2 Kings 4 >