< 2 Kings 11 >

1 Then Athaliah the mother of Ahaziah when she saw that her sonne was dead, she arose, and destroyed all the Kings seede.
Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
2 But Iehosheba the daughter of King Ioram, and sister to Ahaziah tooke Ioash the sonne of Ahaziah, and stale him from among the Kings sonnes that shoulde be slaine, both him and his nource, keeping them in the bed chaber, and they hid him from Athaliah, so that he was not slaine.
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
3 And he was with her hid in the house of the Lord sixe yeere: and Athaliah did reigne ouer the land.
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
4 And the seuenth yeere Iehoiada sent and tooke the captaines ouer hundreths, with other captaines and them of the garde, and caused them to come vnto him into the house of the Lord, and made a couenant with them, and tooke an othe of them in the house of the Lord, and shewed them the Kings sonne.
Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
5 And he commanded them, saying, This is it that ye must doe, The third part of you, that commeth on the Sabbath, shall warde towarde the Kings house:
Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
6 And another third part in the gate of Sur: and another thirde part in the gate behinde them of the garde: and ye shall keepe watche in the house of Massah.
gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
7 And two parts of you, that is, all that goe out on the Sabbath day, shall keepe the watch of the house of the Lord about the King.
Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
8 And ye shall compasse the King rounde about, euery man with his weapon in his hande, and whosoeuer commeth within the ranges, let him be slayne: be you with the King, as he goeth out and in.
Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
9 And the captaines of the hundreths did according to all that Iehoiada the Priest commaded, and they tooke euery man his men that entred in to their charge on the Sabbath with them that went out of it on the Sabbath, and came to Iehoiada the Priest.
Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
10 And the Priest gaue to the captaines of hundreths the speares and the shieldes that were King Dauids, and were in the house of the Lord.
Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
11 And the garde stoode, euery man with his weapon in his hande, from the right side of the house to the left side, about the altar and about the house, round about the King.
Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
12 Then he brought out the Kings sonne, and put the crowne vpon him and gaue him the Testimonie, and they made him King: also they anoynted him, and clapt their handes, and sayde, God saue the King.
Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
13 And when Athaliah heard the noyse of the running of the people, shee came in to the people in the house of the Lord.
Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
14 And when shee looked, beholde, the King stoode by a pillar, as the maner was, and the princes and the trumpetters by the King, and al the people of the land reioyced, and blew with trumpets. Then Athaliah rent her clothes, and cryed, Treason, treason.
Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
15 But Iehoiada the Priest commanded the captaines of the hundreths that had the rule of the hoste, and sayde vnto them, Haue her forth of the ranges, and he that followeth her, let him die by the sworde: for the Priest had sayd, Let her not be slaine in the house of the Lord.
Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
16 Then they laid hands on her, and she went by the way, by the which the horses goe to the house of the King, and there was she slaine.
Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
17 And Iehoiada made a couenant betweene the Lord, and the King and the people, that they should be the Lordes people: likewise betweene the King and the people.
Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
18 Then all the people of the lande went into the house of Baal, and destroyed it with his altars, and his images brake they downe courageously, and slewe Mattan the Priest of Baal before the altars: and the Priest set a garde ouer the house of the Lord.
Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
19 Then he tooke the captaines of hudreths, and the other captaines, and the garde, and all the people of the lande: and they brought the King from the house of the Lord, and came by the way of the gate of the garde to the Kings house: and he sate him downe on the throne of the Kings.
Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
20 And all the people of the land reioyced, and the citie was in quiet: for they had slaine Athaliah with the sworde beside the Kings house.
Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
21 Seuen yeere olde was Iehoash when he began to reigne.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.

< 2 Kings 11 >