< 2 John 1 >

1 THE ELDER to the elect Lady, and her children, whom I loue in the trueth: and not I onely, but also all that haue knowen the trueth,
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi.
2 For the trueths sake which dwelleth in vs, and shalbe with vs for euer: (aiōn g165)
Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn g165)
3 Grace be with you, mercie and peace from God the Father, and from the Lord Iesus Christ the Sonne of the Father, with trueth and loue.
Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
4 I reioyced greatly, that I founde of thy children walking in trueth, as we haue receiued a commandement of the Father.
Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira.
5 And nowe beseeche I thee, Lady, (not as writing a newe commandement vnto thee, but that same which we had from the beginning) that we loue one another.
Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake.
6 And this is that loue, that we should walke after his commandements. This commandement is, that as ye haue heard from the beginning, ye should walke in it.
Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
7 For many deceiuers are entred into this worlde, which confesse not that Iesus Christ is come in the flesh. He that is such one, is a deceiuer and an Antichrist.
Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu.
8 Looke to your selues, that we lose not the things which we haue done, but that we may receiue full reward.
Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.
9 Whosoeuer transgresseth, and abideth not in the doctrine of Christ, hath not God. He that continueth in the doctrine of Christ, he hath both the Father and the Sonne.
Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
10 If there come any vnto you, and bring not this doctrine, receiue him not to house, neither bid him, God speede:
Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni.
11 For he that biddeth him, God speede, is partaker of his euill deedes.
Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.
12 Although I had many things to write vnto you, yet I woulde not write with paper and ynke: but I trust to come vnto you, and speake mouth to mouth, that our ioy may be full.
Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.
13 The sonnes of thine elect sister greete thee, Amen.
Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

< 2 John 1 >